< Psalms 94 >
1 O God, of vengeance, Lord! O God of vengeance, shine forth.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Lift up thyself, O judge of the Earth! bring a recompense upon the proud.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 How long shall the wicked, O Lord—how long shall the wicked exult?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 They sputter, they speak hard things: all the workers of wickedness boast themselves.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Thy people, O Lord! they crush, and thy heritage they afflict.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 The widow and the stranger they slay, and the fatherless they murder.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 And they say, The Lord will not see, and the God of Jacob will not take notice of it.
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Understand, ye brutish among the people: and ye fools, when will ye become intelligent!
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 He that hath planted the ear, shall he not hear? or he that hath formed the eye, shall he not see?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 He that admonisheth nations, shall he not correct? is it not he that teacheth man knowledge!
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 The Lord knoweth the thoughts of man, that they are nought.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Happy is the man whom thou admonisheth, O Lord, and teachest him out of thy law:
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 That thou mayest grant him repose from the days of evil, until the pot be dug for the wicked.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 For the Lord will not cast off his people, and his inheritance will he not forsake.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 For unto righteousness will justice return; and it shall be followed by all the upright in heart.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Who will rise up for me against evil-doers? or who will stand forward for me against the workers of wickedness?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Unless the Lord had been a help unto me, but a little would have been wanting that my soul had dwelt in the silence of death.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 When I said, My foot hath slipped: thy kindness, O Lord, sustained me.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 In the multitude of my [painful] thoughts within me, thy consolations delight my soul.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Can there be associated with thee the throne of destructive wickedness, which frameth mischief as a law?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 They band themselves together against the soul of the righteous, and innocent blood do they condemn.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 But the Lord is become my defence, and my God, the rock of my refuge.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 And he will bring back upon them their own injustice, and in their own wickedness will he destroy them: [yea], he will destroy them—the Lord our God.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.