< Psalms 29 >
1 “A psalm of David.” Ascribe unto the Lord, O ye sons of the mighty, ascribe unto the Lord glory and strength.
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Ascribe unto the Lord the glory of his name; bow down to the Lord in the beauty of holiness.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 The voice of the Lord is upon the waters; the God of glory thundereth, the Lord—upon mighty waters.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 The voice of the Lord [resoundeth] with power; the voice of the Lord [resoundeth] with majesty.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 The voice of the Lord breaketh in pieces the cedars; yea, the Lord shivereth the cedars of Lebanon;
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 And he maketh them skip like a calf; Lebanon and Siryon like young reems.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 The voice of the Lord heweth out flames of fire.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 The voice of the Lord shaketh the wilderness; the Lord shaketh the wilderness of Kadesh.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 The voice of the Lord causeth the hinds to start, and maketh bare forests: and in his temple every thing speaketh [of his] glory.
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 The Lord sat [enthroned] at the flood: and the Lord will sit as King for ever.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 The Lord will give strength unto his people: the Lord will bless his people with peace.
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.