< Psalms 27 >

1 “Of David.” The Lord is my light and my salvation; of whom shall I be afraid? the Lord is the fortress of my life; of whom shall I have dread?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 When evil-doers come near against me to eat up my flesh, my assailants and my enemies at me: then do they stumble and fall.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 If an army should encamp against me, my heart shall not fear: if war should arise against me, even then will I have trust.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 One thing have I asked of the Lord, that I will seek for: that I may dwell in the house of the Lord all the days of my life, to behold the loveliness of the Lord, and to be every morning early in his temple.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 For he will hide me in his pavilion on the day of evil; he will conceal me in the secret of his tabernacle; upon a rock will he place me high.
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 And now will my head be lifted up above my enemies all round about me; and I will sacrifice in his tabernacle sacrifices of joy: I will sing, and I will triumphantly play unto the Lord.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Hear, O Lord, my voice, [when] I call, and be gracious unto me, and answer me.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 Of thee, said my heart, “Seek ye my presence”: thy presence, Lord, will I seek.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Hide [then] not thy face from me; reject not in anger thy servant, thou [who] hast been my help: cast me not off, nor forsake me, O God of my salvation.
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 For my father and my mother have forsaken me; but the Lord will take me up.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Point me out thy way, O Lord! and guide me on a level path, because of those that regard me enviously.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Give me not up to the [revengeful] desire of my assailants; for there are risen up against me false witnesses, and such as utter violence.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 Unless I had believed to see the goodness of the Lord in the land of life—
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Wait on the Lord; be strong, and let thy heart be of good courage; and only wait on the Lord.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.

< Psalms 27 >