< Psalms 17 >
1 “A prayer of David.” Hear, O Lord, [the cause of] righteousness, attend unto my entreaty, give ear unto my prayer, coming from lips without deceit.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 Let from thy presence my sentence come forth; let thy eyes behold what is right.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Thou hast proved my heart; thou hast thought of me in the night; thou hast refined me—thou couldst find nothing: my purpose doth not pass beyond [the words of] my mouth.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 Among the deeds of men did I observe, by the word of thy lips, the paths of the dissolute.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 My steps held firmly to thy tracks, [and] my footsteps did not slip.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 I call on thee, for thou wilt answer me, O God: incline thy ear unto me, hear my speech.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Show marvelously thy loving-kindnesses, O thou that savest those who put their trust [in thee] from those that rise up [against them] by thy right hand.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Keep me as the apple of the eye; conceal me under the shadow of thy wings,
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 From the wicked that despoil me, my enemies, who, to take my life, compass me about.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 They are enclosed in their own fat: with their mouth they speak proudly.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 On our steps they now encompass us: they direct their eyes to turn aside in the land.
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Every man is just like a lion that is greedy to tear his prey, and like a young lion lurking in a covert.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Arise, O Lord, prevent him, cast him down; deliver my soul from the wicked, who is thy sword, —
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 From these men—thy hand—O Lord, from the men of this world, whose portion is in this life, and whose belly thou fillest with thy hidden treasure: they have children in plenty, and leave the rest of their substance to their babes.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 As for me, in righteousness shall I behold thy face: I shall be satisfied, when I awake, with contemplating thy likeness.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.