< Psalms 118 >

1 O give thanks unto the Lord; for he is good; because unto eternity endureth his kindness.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Let Israel then say so; because to eternity endureth his kindness.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Let the house of Aaron then say so; because to eternity endureth his kindness.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Let those who fear the Lord then say so; because to eternity endureth his kindness.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 From the midst of distress I called on the Lord; the Lord answered me with enlargement.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 The Lord is for me; I will not fear: what can a man do unto me?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 The Lord is for me, among those that help me: therefore shall I indeed look on [the punishment of] those that hate me.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 It is better to seek shelter with the Lord than to trust in man.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 It is better to seek shelter with the Lord than to trust in princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 All nations encompassed me about; but in the name of the Lord I will surely cut them off.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 They encompassed me about: yea, they compassed about, but in the name of the Lord I will surely cut them off.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 They encompassed me about like bees; they blazed up like the fire of thorns; but in the name of the Lord I will surely cut them off.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Thou hast thrust violently at me that I might fall; but the Lord assisted me.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 My strength and song is the Lord, and he is become my salvation.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 The voice of rejoicing and salvation is in the tents of the righteous: the right hand of the Lord doth valiantly.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The right hand of the Lord is exalted: the right hand of the Lord doth valiantly.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I shall not die, but I shall live, and relate the works of the Lord.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Severely hath the Lord chastised me; but unto death hath he not given me up.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Open to me the gates of righteousness: I will enter into them. I will give thanks unto the Lord.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 This is the gate which belongeth unto the Lord, the righteous shall enter thereby.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I will thank thee: for thou but answered me, and art become my salvation.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 The stone which the builders rejected is become the chief corner-stone.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 From the Lord is this come to pass, it is marvelous in our eyes.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This is the day which the Lord hath made, we will be glad and rejoice thereon.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 We beseech thee, O Lord, save [us] now: we beseech thee, O Lord, send [us] now prosperity.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Blessed be he that cometh in the name of the Lord: we bless you out of the house of the Lord.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 God is the Lord, and he giveth us light: bind the festive sacrifice with cords, [leading it] up to the horns of the altar.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Thou art my God, and I will thank thee: my God, I will exalt thee.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Oh give thanks unto the Lord; for he is good; because to eternity endureth his kindness.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalms 118 >