< Psalms 112 >

1 Hallelujah. Happy is the man that feareth the Lord, that greatly delighteth in his commandments.
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 His seed shall be mighty upon earth: the generation of the upright shall be blessed.
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Plenty and riches shall be in his house, and his righteousness shall endure for ever.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 There ariseth in the darkness a light to the upright: he is gracious, and merciful, and righteous.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Well will it be with the man who is kind, and lendeth: he will guide his affairs with justice.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 Surely unto eternity shall he not be moved: in everlasting remembrance shall the righteous be held.
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 Of an evil report shall he not be afraid: his heart is firm, trusting in the Lord.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Well supported is his heart, he shall not be afraid, until he looketh on [the punishment of] his assailants.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 He distributeth, he giveth to the needy: his righteousness endureth for ever; his horn shall be exalted in honor.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 The wicked shall see it, and be vexed; he will gnash with his teeth, and melt away: the longing of the wicked shall perish.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

< Psalms 112 >