< Proverbs 6 >
1 My son, If thou hast become surety for thy friend, if thou hast struck thy hand for a stranger;
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 If thou art ensnared through the words of thy mouth, if thou art caught through the words of thy mouth:
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 [Then] do this by all means, my son, and deliver thyself, because thou art come into the power of thy friend, Go hasten to him, and urge thy friend.
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Grant not any sleep to thy eyes, nor slumber to thy eyelids.
Usagone tulo, usawodzere.
5 Deliver thyself as a roebuck from the hand [of the hunter], and as a bird from the hand of the fowler.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Go to the ant, thou sluggard; look on her ways, and become wise.
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 She, that hath no prince, officer, or ruler,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 Provideth in the summer her provision, gathereth in harvest-time her food.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 How long, O sluggard, wilt thou lie down? when wilt thou arise out of thy sleep?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 “A little [more] sleep, a little slumber, a little folding of the hands in lying down;”
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 But then will thy poverty come like a rover, and thy want as a man armed with a shield.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 A Godless person is a man of injustice, who walketh with a distorted mouth.
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 He blinketh with his eyes, he scrapeth with his feet, he pointeth with his fingers;
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 Perverseness is in his heart, he contriveth evil at all times; he scattereth abroad discord.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Therefore shall suddenly come his calamity: unawares shalt he be broken without a remedy.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 Six things there are which the Lord hateth; and seven are an abomination unto his spirit:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 Haughty eyes, a tongue of falsehood, and hands that shed innocent blood,
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 A heart that contriveth plans of injustice, feet that hasten to run after evil,
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 A false witness that eagerly uttereth lies, and him that scattereth abroad discord among brethren.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 Keep, O my son, the commandment of thy father, and reject not the teaching of thy mother:
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Bind them upon thy heart continually, tie them about thy throat.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 When thou walkest, it shall lead thee; when thou liest down, it shall watch over thee; and when thou art awake, it shall converse with thee.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 For the commandment is a lamp, and the law is light; and the way of life are the admonitions of correction:
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 To guard thee against a bad woman, from the flattery of an alien tongue.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Covet not her beauty in thy heart, and let her not conquer thee with her eyelids.
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 For by means of a harlot [one is brought down] to the last loaf of bread: and an adulterous woman will even hunt for the precious life,
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Can a man gather up fire in his lap, and shall his clothes not be burnt?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Can a man walk along upon hot coals, and shall his feet not be burnt?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 So it is with him that goeth in to his neighbor's wife: no one that toucheth her shall remain unpunished.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Men do not despise the thief, if he steal, to gratify his craving when he is hungry:
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 And if he be found, he must pay sevenfold; all the wealth his house must he give.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 But whoso committeth adultery with a woman lacketh sense: he that is the destroyer of his soul, will alone do this.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Plague and disgrace will he meet with; and his reproach will not be blotted out.
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 For jealousy is the fury of a husband, and he will not spare on the day of vengeance.
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 He will not regard the appearance of any ransom; and he will not be content, though thou give ever so many bribes.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.