< Proverbs 5 >
1 My son, attend unto my wisdom; to my understanding incline thou thy ear:
Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
2 That thou mayest observe discretion, and that thy lips may keep knowledge.
kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
3 For as of fine honey drop the lips of an adulterous woman, and smoother than oil is her palate;
Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 But her end is bitter as wormwood, it is sharp as a two-edged sword.
koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 Her feet go down to death, her steps take firm hold on the nether world: (Sheol )
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol )
6 So that she cannot balance the path of life; her tracks are unsteady, and she knoweth it not.
Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 And now, O ye children, hearken unto me, and depart not from the sayings of my mouth.
Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
8 Remove far from her thy way, and come not nigh to the door of her house;
Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
9 That thou mayest not give up unto others thy vigor, and thy years unto the cruel;
kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
10 That strangers may not satisfy themselves with thy strength, and with thy exertions, in the house of an alien:
kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
11 While thou moanest at thy end, when thy flesh and thy body are coming to their end,
Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
12 And thou sayest, How have I hated correction, and how hath my heart rejected reproof;
Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
13 While I hearkened not to the voice of my instructors, and to my teachers I inclined not my ear;
Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
14 But little more was wanting, and I had been in all [kinds of] unhappiness in the midst of the congregation and assembly.
Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
15 Drink water out of thy own cistern, and running waters out of thy own well.
Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
16 So will thy springs overflow abroad; and in the open streets will be thy rivulets of water;
Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
17 They will be thy own only, and not those of strangers with thee.
Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
18 Thy fountain will be blessed: and rejoice with the wife of thy youth, —
Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
19 The lovely gazelle and the graceful chamois: let her bosom satisfy thee abundantly at all times; with her love be thou ravished continually.
Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
20 And why wilt thou, my son, be ravished with an adulteress, and embrace the bosom of an alien woman?
Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
21 For before the eyes of the Lord are the ways of man, and all his tracks doth he weigh in the balance.
Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
22 His own iniquities will truly catch the wicked, and with the cords of his sin will he be held firmly.
Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
23 He will indeed die for want of correction; and through the abundance of his folly will he sink into error.
Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.