< Numbers 36 >

1 And there came near the chiefs of the divisions of the family of the children of Gil'ad, the son of Machir, the son of Menasseh, of the families of the sons of Joseph; and they spoke before Moses, and before the princes, the chiefs of the divisions of the children of Israel;
Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
2 And they said, the Lord hath commanded my Lord to give the land for an inheritance by lot to the children of Israel; and my Lord hath been commanded by the Lord to give the inheritance of Zelophehad our brother unto his daughters.
Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
3 And if they become the wives of any of the sons of the [other] tribes of the children of Israel: then will their inheritance be taken from the inheritance of our fathers, and be added to the inheritance of the tribe whereamong they may be married; and from the lot of our inheritance will it be taken away.
Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
4 And whenever the jubilee shall be to the children of Israel: then will their inheritance be added unto the inheritance of the tribe whereamong they may be married; and from the inheritance of the tribe of our fathers will their inheritance be taken away.
Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
5 And Moses commanded the children of Israel by the order of the Lord, saying, the tribe of the sons of Joseph have spoken well.
Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
6 This is the thing which the Lord hath commanded concerning the daughters of Zelophehad, saying, To those who are pleasing in their eyes may they become wives; however only to the family of the tribe of their father shall they become wives.
Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
7 And the inheritance of the children of Israel shall not pass from tribe to tribe; but the children of Israel shall adhere every one to the inheritance of the tribe of his fathers.
kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
8 And every daughter that inheriteth any possession out of any tribe of the children of Israel, shall become the wife unto one of the family of the tribe of her father; in order that the children of Israel may inherit every one the inheritance of his fathers.
Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
9 And no inheritance shall pass from one tribe to another tribe; but the tribes of the children of Israel shall adhere, every one, to his own inheritance.
Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
10 Even as the Lord had commanded Moses, so did the daughters of Zelophehad;
Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
11 And Machlah, Tirzah, and Choglah, and Milcah, and No'ah, the daughters of Zelophehad became the wives of the sons of their uncles.
Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
12 [To persons] of the families of the sons of Menasseh the son of Joseph did they become wives, and their inheritance remained in the tribe of the family of their father.
Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
13 These are the commandments and the ordinances, which the Lord commanded by the hand of Moses unto the children of Israel, in the plain of Moab by the Jordan opposite Jericho.
Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.

< Numbers 36 >