< Numbers 20 >

1 And the children of Israel, the whole congregation, came into the desert of Zin in the first month, and the people abode in Kadesh; and Miriam died there, and was buried there.
Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.
2 And there was no water for the congregation; and they assembled themselves together against Moses and against Aaron.
Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni.
3 And the people quarreled with Moses, and said thus, Oh that we had but perished when our brethren perished before the Lord!
Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova!
4 And why have ye brought the congregation of the Lord into this wilderness, to die there, we and our cattle!
Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno?
5 And wherefore have ye caused us to come up out of Egypt, to bring us in unto this evil place? it is no place for sowing, or of figs, or of vines, or of pomegranates; and water even there is none to drink.
Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”
6 And Moses and Aaron went from the presence of the assembly unto the door of the tabernacle of the congregation, and they fell upon their faces: and the glory of the Lord appeared unto them.
Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
7 And the Lord spoke unto Moses, saying,
Yehova anati kwa Mose,
8 Take the staff, and gather the assembly together, thou, with Aaron thy brother, and ye shall speak unto the rock before their eyes, that it shall give forth its water; and thou shalt bring forth for them water out of the rock, and give drink to the congregation and their cattle.
“Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”
9 And Moses took the staff from before the Lord, as he had commanded him.
Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira.
10 And Moses and Aaron assembled the congregation together before the rock, and he said unto them, Hear now, ye rebels! shall we out of this rock bring forth water for you?
Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?”
11 And Moses lifted up his hand, and he smote the rock with his staff twice: and there came out much water, and the congregation drank, together with their cattle.
Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.
12 And the Lord said unto Moses and Aaron, Because ye have not confided in me, to sanctify me before the eyes of the children of Israel: therefore shall ye not bring this congregation into the land which I have given to them.
Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”
13 These are the waters of Meribah; where the children of Israel quarreled with the Lord, and through which he was sanctified.
Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.
14 And Moses sent messengers from Kadesh unto the king of Edom, Thus hath said thy brother Israel, Thou knowest all the hardship that hath befallen us.
Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti, “Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera.
15 How our fathers went down into Egypt, and we dwelt in Egypt many days; and the Egyptians did evil to us, and to our fathers:
Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo,
16 And we cried unto the Lord, and he heard our voice, and he sent a messenger, and caused us to go forth out of Egypt; and, behold, we are in Kadesh, a city at the outmost end of thy border.
koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.” “Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu.
17 Let us pass, we pray thee, through thy country; we will not pass through field, or through vineyard, and we will not drink the water of the wells: by the king's highway will we go, we will not turn to the right hand nor to the left, until we have passed thy border.
Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
18 And Edom said unto him, Thou shalt not pass through my land, lest I come against thee with the sword.
Koma Edomu anayankha kuti, “Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”
19 And the children of Israel said unto him, We will go by the highway: and if we drink of thy water, I and my cattle, then will I pay its value; I will do thee no injury, only on foot will I pass through.
Aisraeli anayankha kuti, “Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”
20 And he said, Thou shalt not pass through; and Edom came out against him with much people, and with a strong hand.
Koma Edomu anayankhanso kuti, “Musadutse.” Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu.
21 And as Edom thus refused to permit Israel to pass through his border, Israel turned away from him.
Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.
22 And they set forward from Kadesh; and the children of Israel, the whole congregation, came unto mount Hor.
Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori.
23 And the Lord said unto Moses and Aaron at mount Hor, by the boundary of the land of Edom, as followeth,
Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
24 Aaron shall be gathered unto his people; for he shall not enter into the land which I have given unto the children of Israel, because ye rebelled against my order at the waters of Meribah.
“Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba.
25 Take Aaron and Elazar, his son, and cause them to go up unto mount Hor:
Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori.
26 And cause Aaron to take off his garments, and clothe therewith Elazar his son; and Aaron shall be gathered in, and he shall die there.
Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”
27 And Moses did as the Lord had commanded; and they went up to mount Hor before the eyes of all the congregation.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona.
28 And Moses caused Aaron to take off his garments, and he clothed therewith Elazar his son; and Aaron died there on the top of the mount; and Moses and Elazar then came down from the mount.
Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko,
29 And when all the congregation saw that Aaron was departed, they wept for Aaron thirty days, even all the house of Israel.
ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.

< Numbers 20 >