< Numbers 15 >
1 And the Lord spoke unto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speak unto the children of Israel and say unto them, When ye shall have come into the land of your habitations, which I give unto you,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
3 And ye will prepare a fire-offering unto the Lord, a burnt-offering, or a sacrifice, in performing a pronounced vow, or as a freewill-offering, or on your solemn feasts, to prepare a sweet savor unto the Lord, of the herds of the flocks:
ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
4 Then shall he that bringeth his offering unto the Lord, bring as a meat-offering a tenth part of fine flour mingled with the fourth of a hin of oil.
munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
5 And wine for a drink-offering, the fourth of a hin, shalt thou prepare with the burnt-offering or sacrifice, for each one sheep.
Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
6 But for a ram, shalt thou prepare as a meat-offering two tenth parts of fine flour mingled with the third of a hin of oil.
“Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
7 And wine for the drink-offering, the third of a hin, shalt thou bring, for a sweet savor unto the Lord.
ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
8 And when thou preparest a bullock for a burnt-offering, or for a sacrifice, in performing a pronounced vow, or a peace-offering unto the Lord:
“‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
9 Then shall he bring with the bullock as a meat-offering, three tenth parts of fine flour mingled with half a hin of oil.
pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
10 And wine shalt thou bring for a drink-offering, half a hin, as a fire-offering of a sweet savor unto the Lord.
Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
11 Thus shall it be done for each one bullock, or for each one ram, or for a lamb, be it of the sheep or of the goats.
Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
12 According to the number that ye may prepare, so shall ye do to every one according to their number.
Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
13 All that are born in the country shall do these things after this manner, in offering a fire-offering of a sweet savor unto the Lord.
“‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
14 And if a stranger sojourn with you, or whosoever may be among you in your generations, and will make an offering made by fire, of a sweet savor unto the Lord: as ye do, so shall he do.
Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
15 Congregation! one statute shall be for you, and for the stranger that sojourneth: a statute for ever in your generations; as ye are, so shall the stranger be before the Lord.
Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
16 One law and one code shall be for you, and for the stranger that sojourneth with you.
Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
17 And the Lord spoke unto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Speak unto the children of Israel, and say unto them, When ye come into the land whither I bring you:
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
19 Then shall it be, that, when ye eat of the bread of the land, ye shall set aside a heave-offering unto the Lord.
ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
20 As the first of your doughs shall ye set aside a cake for a heave-offering; like the heave-offering of the threshing-floor, so shall ye set this aside.
Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
21 Of the first of your doughs shall ye give unto the Lord a heave-offering, in your generations.
Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
22 And if ye err, and do not observe all these commandments, which the Lord hath spoken unto Moses,
“‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
23 All that the Lord hath commanded you by the hand of Moses, from the day that the Lord commanded [the same] and thenceforward, among your generations:
lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
24 Then shall it be, if, through inadvertence of the congregation, it was committed by ignorance, that all the congregation shall prepare one young bullock for a burnt-offering, for a sweet savor unto the Lord, with his meat-offering, and his drink-offering, according to the prescribed manner, and one he-goat for a sin-offering.
ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
25 And the priest shall make an atonement for all the congregation of the children of Israel, and it shall be forgiven unto them; for it is [a sin of] ignorance; and they have brought their offering, a sacrifice made by fire unto the Lord, and their sin-offering before the Lord, for their [sin of] ignorance:
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
26 And it shall be forgiven unto all the congregation of the children of Israel, and unto the stranger that sojourneth among them; for by all the people [was it done] in ignorance.
Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
27 And if any person sin through ignorance, then shall he bring a she-goat of the first year for a sin-offering.
“‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
28 And the priest shall make an atonement for the person that hath erred, in his sinning through ignorance before the Lord; to make an atonement for him, that it may be forgiven unto him.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
29 For the native born among the children of Israel, and for the stranger that sojourneth among them: —one law shall be for you, for him that acteth through ignorance.
Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
30 But the person that doth aught with a high hand, be he one born in the land, or a stranger, the same dishonoreth the Lord; and that person shall be cut off from among his people.
“‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
31 Because the word of the Lord hath he despised, and his commandment hath he broken; that person shall be cut off, his iniquity is upon him.
Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
32 And while the children of Israel were in the wilderness, they found a man gathering sticks upon the sabbath-day.
Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
33 And they that found him gathering sticks brought him for judgment unto Moses and Aaron, and unto all the congregation.
Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
34 And they put him in ward; because it had not been declared what should be done to him.
ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
35 And the Lord said unto Moses, The man shall be put to death: all the congregation shall stone him with stones without the camp.
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
36 And all the congregation brought him forth to without the camp, and they stoned him with stones, and he died; as the Lord had commanded Moses.
Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
37 And the Lord said unto Moses, as followeth,
Yehova anawuza Mose kuti,
38 Speak unto the children of Israel, and say to them, that they shall make themselves fringes on the corners of their garments throughout their generations, and that they shall put upon the fringe of the corner a thread of blue:
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
39 And it shall be unto you for a fringe, that ye may look upon it, and remember all the commandments of the Lord, and do them; and that ye seek not after [the inclination of] your own heart and [the delight of] your eyes, in pursuit of which ye have been led astray.
Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
40 In order that ye may remember, and do all my commandments, and be holy unto your God.
Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
41 I am the Lord your God, who brought you out of the land of Egypt, to be your God: I am the Lord your God.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”