< Nehemiah 1 >

1 The words of Nehemiah the son of Chachalyah. And it came to pass in the month Kislev, in the twentieth year, as I was in Shushan, the capital,
Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
2 That there came Chanani, one of my brethren, himself with certain men of Judah: and I asked them concerning the Jews that had escaped, who were left of the captivity, and concerning Jerusalem.
Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
3 And they said unto me, The remnant that are left of the captivity there in the province are in great misery and in disgrace; and the wall of Jerusalem is broken down, and her gates are burnt with fire.
Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
4 And it came to pass, when I heard these words, that I sat down and wept, and mourned some days, and I was fasting, and praying before the God of heaven.
Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
5 And I said, I beseech thee, O Lord the God of heaven, the great and terrible God, that keepeth the covenant and kindness for those that love him and for those that keep his commandments:
Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
6 Let thy ear now be attentive, and thy eyes be open, I entreat thee, to hearken unto the prayer of thy servant, which I am praying this day before thee, by day and by night, in behalf of the children of Israel thy servants, and [as] I confess for the sins of the children of Israel, [with] which we have sinned against thee: yea, I also and my father's house have sinned.
Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
7 We have dealt very corruptly toward thee: and we have not kept the commandments, and the statutes, and the ordinances, which thou didst command Moses thy servant.
Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
8 Remember, I beseech thee, the word with which thou didst charge Moses thy servant, saying, If ye become truly unfaithful, I will indeed scatter you among the nations.
“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
9 But if ye return unto me, and keep my commandments, and do them: [then] though your outcasts should be at the utmost parts of heaven, from there will I gather them, and I will bring them unto the place which I have chosen to let my name dwell there.
Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
10 And they are thy servants and thy people, whom thou hast redeemed by thy great power, and by thy strong hand.
“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
11 I beseech thee, O Lord, do let thy ear be attentive to the prayer of thy servant, and to the prayer of thy servants, who are desirous to fear thy name; and grant success, I pray thee, to thy servant this day, and let him find mercy in the sight of this man —But I was butler by the king.
Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

< Nehemiah 1 >