< Micah 2 >
1 Woe to those that devise wickedness, and resolve on evil upon their couches! by the first light of the morning they execute it, if they have it in the power of their hand.
Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
2 And they covet fields, and rob them; and houses, and take them away: so they defraud the master and his house, and the man and his heritage.
Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
3 Therefore thus hath said the Lord, Behold, I will devise against this family an evil, from which ye shall not remove your necks; nor shall ye go erect; for it is an evil time.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
4 On that day shall one take up a parable against you, and lament with a mournful lamentation, and say, “We are utterly wasted: the portion of my people hath he exchanged; how hath he removed it from me! instead of restoring [them to us] he divideth our fields.”
Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
5 Therefore shalt thou have none that shall draw the [measuring] cord in [his] lot in the congregation of the Lord.
Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
6 “Preach not;” [but] they shall preach: they shall not preach [indeed] to these, that reproach may not overtake them.
Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
7 Shall it be said [in] the house of Jacob, Is the spirit of the Lord straightened? are these his doings? Do not my words do good to him that walketh uprightly?
Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
8 But long since is my people risen up as an enemy: from the garment do you pull off the ornament; of those that pass by securely [ye make] men returned from war.
Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
9 The wives of my people do you drive out of their delightful houses; from their children do ye take away my ornament for ever.
Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
10 Arise ye, and depart; for this is not your resting-place; because it is polluted, it shall destroy [you], even with a grievous destruction.
Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
11 If a man that goeth after wind and lieth with falsehood [should say], “I will preach unto thee of wine and of strong drink:” he would be a preacher for this people.
Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
12 I will [once] surely assemble, O Jacob, all of thee; I will surely gather up the remnant of Israel; I will place them together as flocks in the fold, as droves in the midst of their pen: they shall be crowded with men.
“Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
13 The wall-breaker cometh up before them; they break in and pass through the gate, and go out by it: and their king passeth on before them, and the Lord at their head.
Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”