< Leviticus 25 >

1 And the Lord spoke unto Moses on mount Sinai, saying,
Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
2 Speak unto the children of Israel, and say unto them, When ye come into the land which I give unto you; then shall the land keep a sabbath unto the Lord.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
3 Six years shalt thou sow thy field, and six years shalt thou prune thy vineyard, and gather in the fruit thereof;
Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
4 But in the seventh year there shall be a sabbath of rest unto the land, a sabbath [in honor] of the Lord: thy field shalt thou not sow, and thy vineyard shalt thou not prune.
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
5 That which groweth of its own accord of thy harvest shalt thou not reap, and the grapes of thy undressed vine shalt thou not gather: a year of rest shall it be unto the land.
Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
6 And [the product of] the sabbath of the land shall be unto you for food, for thee, and for thy man-servant, and for thy maid-servant, and for thy hired laborer, and for thy stranger, that sojourn with thee;
Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
7 And for thy cattle, and for the beasts that are in thy land, shall all its products be [left] for food.
Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
8 And thou shalt number unto thee seven sabbaths of years, seven years seven times; and the space of the seven sabbaths of years shall be unto thee forty and nine years.
“‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
9 And then shalt thou cause the sound of the cornet to be heard, in the seventh month, on the tenth day of the month: on the day of atonement shall ye sound the cornet throughout all your land.
Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
10 And ye shall hallow the fiftieth year, and proclaim freedom throughout the land unto all the inhabitants thereof; it shall be a jubilee unto you; and ye shall return, every man, unto his possession, and ye shall return, every man, unto his family.
Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
11 A jubilee shall this, the fiftieth year, be unto you: ye shall not sow, nor reap that which groweth of itself in it, nor gather in it the fruit of the undressed vines.
Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
12 For it is the jubilee; holy shall it be unto you: from the field shall ye eat the products thereof.
Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
13 In this year of the jubilee shall ye return, every man, unto his possession.
“‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
14 And if thou sell aught unto thy neighbor, or buy aught of thy neighbor's hand, ye shall not overreach one the other;
“‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
15 According to the number of years after the jubilee shalt thou buy of thy neighbor, according unto the number of harvest-years shall he sell unto thee;
Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
16 According to the multitude of years shalt thou increase the price thereof, and according to the fewness of years shalt thou diminish the price thereof; for a number of harvests doth he sell unto thee.
Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
17 And ye shall not overreach one the other; but thou shalt be afraid of thy God; for I am the Lord your God.
Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
18 And ye shall do my statutes, and my ordinances shall ye keep and do them; and then shall ye dwell in the land in safety.
“‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
19 And the land shall yield its fruit, and ye shall eat your fill, and dwell in safety therein.
Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
20 And if ye should say, What shall we eat in the seventh year? behold, we are not permitted to sow, and we cannot gather in our harvest:
Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
21 Then will I command my blessing unto you in the sixth year, and it shall bring forth a harvest for three years.
Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
22 And when ye sow in the eighth year, then shall ye eat yet of the old harvest; until the ninth year, until its harvest come in, shall ye eat of the old store.
Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
23 And the land shall not be sold for a permanence [to the purchaser]; for the land is mine; for strangers and sojourners are ye with me.
“‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
24 And in all the land of your possession ye shall grant a redemption for the land.
Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
25 If thy brother become poor, and sell away some of his possession: then may his nearest of kin come and redeem what his brother hath sold.
“‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
26 And if the man have none to redeem it, and he acquire the means, sufficient to be able to redeem it himself:
Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
27 Then let him reckon the years since his sale, and restore the overplus unto the man to whom he sold it; and so shall he return unto his possession.
Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
28 But if his means do not suffice to enable him to restore it to him: then shall that which he hath sold remain in the hand of him that hath bought it until the year of the jubilee; and it shall be freed in the jubilee, and he shall return unto his possession.
Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
29 And if a man sell a dwelling-house in a walled city: then shall the time of redemption last till the end of the year of his sale; a full year shall his time of redemption last.
“‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
30 And if it be not redeemed within the expiration of a full year: then shall the house which is in the walled city remain as a permanence to him that bought it throughout his generations; it shall not become freed in the jubilee.
Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
31 But the houses of the villages which have no wall round about them shall be counted as the fields of the country: they shall have the right of redemption, and they shall become freed in the jubilee.
Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
32 And [respecting] the cities of the Levites, the houses of the cities of their possession, a perpetual right of redemption shall belong to the Levites.
“‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
33 And if a man of the Levites redeem something: then shall the house that was sold, and the city of his possession, become freed in the jubilee; for the houses of the cities of the Levites are their possession among the children of Israel.
Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
34 And a field of the suburbs of their cities shall not be sold; for a perpetual possession is it unto them.
Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
35 And if thy brother become poor, and fall in decay with thee: then shalt thou assist him, [yea] a stranger, or a sojourner, that he may live with thee.
“‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
36 Thou shalt not take of him any usury or increase; but thou shalt be afraid of thy God: that thy brother may live with thee.
Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
37 Thy money shalt thou not give him upon usury, nor lend him thy victuals for increase.
Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
38 I am the Lord your God, who have brought you forth out of the land of Egypt, to give unto you the land of Canaan, to be unto you a God.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
39 And if thy brother become poor near thee, and be sold unto thee: thou shalt not compel him to work as a bond-servant.
“‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
40 But as a hired laborer, as a sojourner, shall he be with thee; until the year of the jubilee shall he serve with thee:
Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
41 And then shall he depart from thee, he and his children with him; and he shall return unto his own family, and unto the possession of his fathers shall he return.
Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
42 For my servants are they, whom I brought forth out of the land of Egypt: they shall not be sold as bond-men are sold.
Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
43 Thou shalt not rule over him with rigor; but thou shalt have fear of thy God.
Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
44 But thy bond-man, and thy bond-woman that shall remain thine, shall be of the nations that are round about you; of them may ye buy bond-man and bond-woman.
“‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
45 And also of the children of the strangers that sojourn with you, of them may ye buy, and of their families that are with you, which they have begotten in your land; and they shall remain to you as a possession.
Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
46 And ye may transfer them as an inheritance for your children after you, to inherit them for a possession; you may hold them to service for ever; but over your brethren the children of Israel, one over the other, ye shall not rule with rigor.
Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
47 And if a stranger or sojourner wax rich near thee, and thy brother become poor near him, and he sell himself unto the sojourning stranger near thee, or to a descendant of a stranger's family:
“‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
48 After he hath sold himself shall he have the right of redemption; one of his brethren may redeem him.
wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
49 Either his uncle, or his uncle's son, may redeem him, or any that is near of kin unto him of his family may redeem him; or if he obtain the means, he may redeem himself.
amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
50 And he shall reckon with him that bought him from the year that he sold himself to him unto the year of the jubilee: and the price of his sale shall be according to the number of years, as the time of a hired laborer shall he have been with him.
Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
51 If there be yet many years, according to them shall he return the price of his redemption out of his purchase-money.
Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
52 And if there remain but few years unto the year of the jubilee: then shall he reckon with him; according to his years shall he return the price of his redemption.
Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
53 As a laborer hired from year to year shall he be with him; he shall not rule over him with rigor before thy eyes.
Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
54 And if he be not redeemed by [one of] these means: then shall he go out in the year of the jubilee, both he, and his children with him.
“‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
55 For unto me are the children of Israel servants, my servants are they, whom I have brought forth out of the land of Egypt: I am the Eternal your God.
pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

< Leviticus 25 >