< Lamentations 2 >

1 Oh how hath the Lord covered in his anger the daughter of Zion with a cloud; he hath cast down from heaven unto the earth the ornament of Israel; and he hath not remembered his footstool on the day of his anger!
Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
2 The Lord hath destroyed and hath not pitied all the habitation of Jacob: he hath thrown down in his wrath the strong-holds of the daughter of Judah: he hath thrown them down to the ground; he hath defiled the kingdom and its princes.
Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
3 He hath hewn away in his fierce anger the whole horn of Israel; he hath drawn back his right hand before the enemy; and he burnt against Jacob like a flaming fire, which devoureth round about.
Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4 He bent his bow like an enemy; he held out his right hand as an adversary, and slew all that were pleasant to the eye: in the tent of the daughter of Zion did he pour out like fire his fury.
Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5 The Lord became like an enemy; he destroyed Israel, he destroyed all her palaces, he ruined her strong-holds, and he increased in the midst of the daughter of Judah groaning and wailing.
Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6 And he violently wasted, as if it were a garden, his tabernacle; he destroyed his place of assembly: [yea, ] the Lord hath caused to be forgotten in Zion the solemn feast and the day of rest, and hath despised in the indignation of his anger both king and priest.
Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
7 The Lord hath cast off his altar, he hath made void his sanctuary, he hath surrendered into the hand of the enemy the walls of her palaces: they have made their voice to resound in the house of the Lord, as on a day of a solemn feast.
Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8 The Lord hath resolved to destroy the wall of the daughter of Zion; he stretched out the measuring-line, he withdrew not his hand from destroying: and he caused the rampart and the wall to mourn; together they languish.
Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
9 Sunk into the ground are her gates, he hath ruined and broken her bars: her king and her princes are among the nations without any law; her prophets also obtain no more any vision from the Lord.
Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10 The elders of the daughter of Zion sit upon the ground, they keep silence: they have thrown dust upon their head; they have girt themselves with sackcloth: the virgins of Jerusalem have brought down low their head to the ground.
Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
11 My eyes do fail with tears, my bowels are heated, my liver is poured upon the earth because of the breach of the daughter of my people; because babes and sucklings faint away in the streets of the town.
Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
12 To their mothers they say, Where is corn and wine? when they faint away like the deadly wounded in the streets of the city, when their soul is poured out on the bosom of their mother.
Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
13 What shall I take to witness for thee? what shall I compare unto thee, O daughter of Jerusalem? what shall I find equal to thee, that I may comfort thee, O virgin daughter of Zion? for great like the sea is thy breach; who can bring healing to thee?
Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
14 Thy prophets foresaw for thee vain and deceptive things; and they did not lay open thy iniquity, to cause thy backsliders to return: but they foresaw for thee prophecies of falsehood and seduction.
Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
15 All that pass by [this] way clap their hands on account of thee; they hiss and shake their head over the daughter of Jerusalem: [saying, ] Is this the city that men called The perfection of beauty. The joy for all the earth?
Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16 All thy enemies open wide their mouth against thee; they hiss and gnash their teeth; they say, We have swallowed her up: ah, truly this is the day that we hoped for; we have found, we have seen it.
Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
17 The Lord hath done what he had resolved; he hath accomplished his word which he had ordained already in the days of old; he hath thrown down, and hath not pitied; and he hath caused to rejoice over thee thy enemy, he hath raised on high the horn of thy adversaries.
Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
18 Their heart crieth unto the Lord, O thou wall of the daughter of Zion, let tears run down like a stream day and night; allow thyself no rest; let not the apple of thy eye be still.
Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19 Arise, complain aloud in the night, in the beginning of the watches; pour out like water thy heart before the face of the Lord: lift up toward him thy hands because of the life of thy babes, that faint away for hunger at the corner of all the streets.
Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20 See, O Lord, and behold! to whom hast thou ever done the like? Shall women, then, eat their own fruit, the babes they have tenderly nursed? or shall there be slain in the sanctuary of the Lord the priest and the prophet?
Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
21 There lie down on the ground in the streets the lad and the ancient: my virgins and my young men are fallen by the sword: thou hast slain on the day of thy anger; thou hast slaughtered, thou hast not pitied.
Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
22 Thou hast called, as it were on a festive day, my evil neighbors from round about; and there was not on the day of the Lord's anger one that escaped or remained: those that I had tenderly nursed and reared up my enemy brought to their end.
Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.

< Lamentations 2 >