< Judges 1 >
1 And it came to pass after the death of Joshua, that the children of Israel asked the Lord, saying, Who shall go up for us against the Canaanites at the first, to fight against them?
Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
2 And the Lord said, Judah shall go up; behold, I have delivered the land into his hand.
Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
3 And Judah said unto Simeon his brother, Come up with me into my lot, and we will fight against the Canaanites; and I likewise will go with thee into thy lot. So Simeon went with him.
Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
4 And Judah went up; and the Lord delivered the Canaanites and the Perizzites into their hand; and they smote [of] them in Bezek ten thousand men.
Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
5 And they found Adoni-bezek in Bezek; and they fought against him, and they smote the Canaanites and the Perizzites.
Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
6 But Adoni-bezek fled; and they pursued after him, and caught him, and cut off his thumbs and his great toes.
Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
7 And Adoni-bezek said, Seventy kings, having their thumbs and their great toes cut off, gathered food under my table: as I have done, so hath God requited me. And they brought him to Jerusalem, and he died there.
Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
8 And the children of Judah fought against Jerusalem, and captured it, and they smote it with the edge of the sword, and the city they set on fire.
Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
9 And afterward did the children of Judah go down to fight against the Canaanites, that dwelt in the mountain, and in the south, and in the lowlands.
Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
10 And Judah went against the Canaanites that dwelt in Hebron; [now the name of Hebron was formerly Kiryath-arba'; ] and they smote Sheshai, and Achiman, and Talmai.
Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
11 And he went from there against the inhabitants of Debir; and the name of Debir was formerly Kiryath-sepher:
Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
12 And Caleb said, He that will smite Kiryath-sepher, and capture it, to him will I give 'Achsah my daughter for wife.
Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
13 And 'Othniel the son of Kenaz, Caleb's younger brother, captured it: and he gave him 'Achsah his daughter for wife.
Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
14 And it came to pass, when she came to him, that she persuaded him to ask of her father a field: and she alighted from off her ass; and Caleb said unto her, What aileth thee?
Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
15 And she said unto him, Give me a blessing; for thou hast given me a dry land: give me also springs of water. And Caleb gave her the upper springs and the nether springs.
Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
16 And the children of the Kenite, the father-in-law of Moses, went up out of the city of palm-trees with the children of Judah into the wilderness of Judah, which is at the south of 'Arad; and they went and dwelt with the people.
Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
17 And Judah went with Simeon his brother, and they smote the Canaanites that inhabited Zephath, and devoted it. And the name of the city was called Chormah.
Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
18 And Judah captured Gazzah with its territory, and Ashkelon with its territory, and 'Ekron with its territory.
Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
19 And the Lord was with Judah; and he took possession of the mountain; but could not drive out the inhabitants of the valley, because they had chariots of iron.
Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
20 And they gave Hebron unto Caleb, as Moses had spoken; and he drove out thence the three sons of 'Anak.
Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
21 And the Jebusites that inhabited Jerusalem, the children of Benjamin did not drive out; but the Jebusites dwelt with the children of Benjamin in Jerusalem until this day.
Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
22 And the house of Joseph, these also, went up against Beth-el; and the Lord was with them.
A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
23 And the house of Joseph sent to spy out Beth-el: now the name of the city formerly was Luz.
Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
24 And the watchers saw a man coming forth out of the city, and they said unto him, Show us, we pray thee, the entrance into the city, and we will show thee kindness.
Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
25 And he showed them the entrance into the city, and they smote the city with the edge of the sword; but the man and all his family they let go free.
Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
26 And the man went into the land of the Hittites, and built a city, and called its name Luz: this is its name unto this day.
Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
27 Neither did Menasseh drive out [the inhabitants of] Beth-shean and its towns, nor Ta'anach and its towns, nor the inhabitants of Dor and its towns, nor the inhabitants of Yible'am and its towns, nor the inhabitants of Megiddo and its towns; but the Canaanites succeeded to remain in this land.
Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
28 And it came to pass, when Israel became strong, that they put the Canaanites to tribute; but they did not drive them out entirely.
Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
29 Neither did Ephraim drive out the Canaanites that dwelt in Gezer; and the Canaanites dwelt in the midst of them at Gezer.
Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
30 Zebulun did not drive out the inhabitants of Kitron, nor the inhabitants of Nahalol; and the Canaanites dwelt in the midst of them, and became tributary.
Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
31 Asher did not drive out the inhabitants of 'Akko, nor the inhabitants of Zidon, nor of Achlab, nor of Achzib, nor of Chelbah, nor of Aphik, nor of Rechob;
A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
32 And the Asherites dwelt in the midst of the Canaanites, the inhabitants of the land; for they did not drive them out.
Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
33 Naphtali did not drive out the inhabitants of Beth-shemesh, nor the inhabitants of Beth-'anath; and he dwelt in the midst of the Canaanites, the inhabitants of the land; nevertheless the inhabitants of Beth-shemesh and of Beth-anath became tributary unto them.
Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
34 And the Emorites forced the children of Dan into the mountain; for they would not suffer them to come down into the valley;
Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
35 And the Emorites succeeded to remain on mount Cheres, in Ayalon, and in Sha'albim; but when the hand of the house of Joseph prevailed, they became tributary.
Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
36 And the territory of the Emorites was from the ascent of 'Akrabbim, from the Rock upward.
Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.