< Judges 9 >

1 And Abimelech the son of Yerubba'al went to Shechem unto his mother's brothers, and spoke unto them, and unto all the family of the house of his mother's father, saying,
Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
2 Speak, I pray you, in the ears of all the men of Shechem, What is better for you, either that there should rule over you seventy men, all the sons of Yerubba'al, or that there reign over you one man? and remember that I am your bone and your flesh.
“Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
3 And his mother's brothers spoke concerning him in the ears of all the men of Shechem all these words; and their heart became inclined after Abimelech; for they said, He is our brother.
Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
4 And they gave him seventy pieces of silver out of the house of Ba'al-berith; and Abimelech hired therewith idle and heedless persons, who followed him.
Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
5 And he came unto his father's house at 'Ophrah, and slew his brothers the sons of Yeruhba'al, seventy persons, upon one stone; and there was yet left Yotham the youngest son of Yerubba'al; for he had hidden himself.
Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
6 And all the men of Shechem and all Beth-millo assembled together, and went, and made Abimelech king, by the oak of the pillar that was by Shechem.
Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
7 And they told it to Yotham; and he went and stood on the top of mount Gerizzim, and he lifted up his voice, and cried; and he said unto them, Hearken unto me, ye men of Shechem, so that God may hearken unto you.
Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
8 The trees went once forth to anoint a king over them; and they said unto the olive-tree, Reign thou over us.
Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
9 But the olive-tree said unto them, Should I give up my fatness, wherewith through me they honor God and men, and shall I go to be promoted over the trees!
“Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
10 And the trees said to the fig-tree, Come thou, reign over us.
Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
11 But the fig-tree said unto them, Should I give up my sweetness, and my good productiveness, and go to be promoted over the trees?
Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
12 Then said the trees unto the vine, Come thou, reign over us.
Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
13 But the vine said unto them, Should I give up my fresh wine, which rejoiceth God and men, and go to be promoted over the trees!
Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
14 Then said all the trees unto the bramble, Come thou, reign over us.
Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
15 And the bramble said unto the trees, If in truth ye anoint me as king over you, then come seek protection in my shadow; and if not, then let fire come out of the bramble, and devour the cedars of the Lebanon.
Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
16 And now, if ye have acted in truth and sincerity, when ye made Abimelech king, and if ye have dealt well with Yerubba'al and his house, and have done unto him according to the merit of his hands;
Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
17 (In that my father fought for you, and cast his life far away, and delivered you out of the hand of Midian;
Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
18 While ye are risen up against my father's house this day, and have slain his sons, seventy men, upon one stone, and have made Abimelech, the son of his maid-servant, king over the men of Shechem, because he is your brother; )
Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
19 If ye have thus acted in truth and sincerity with Yerubba'al and with his house this day: then rejoice ye in Abimelech, and let him also rejoice in you.
Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
20 But if not, let fire come out from Abimelech, and devour the men of Shechem and Beth-millo; and let fire come out from the men of Shechem, and from Beth-millo, and devour Abimelech.
Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
21 And Yotham ran away, and fled, and went to Beer, and dwelt there, for fear of Abimelech his brother.
Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
22 And Abimelech ruled over Israel three years;
Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
23 And then did God send an evil spirit between Abimelech and the men of Shechem; and the men of Shechem became unfaithful toward Abimelech;
Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
24 So that the violence [done] to the seventy sons of Yerubba'al might come, and their blood be laid upon Abimelech their brother, who had slain them; and upon the men of Shechem, who had strengthened his hands to slay his brothers.
Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
25 And the men of Shechem set persons to lie in wait for him on the tops of the mountains, and they robbed all that passed by them on that way: and it was told unto Abimelech.
Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
26 And there came Ga'al the son of 'Ebed with his brothers, and passed through Shechem: and the men of Shechem put their confidence in him.
Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
27 And they went out into the field, and gathered their vineyards, and trod [the grapes], and made joyful feasts, and went into the house of their god, and ate and drank, and cursed Abimelech.
Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
28 And Ga'al the son of 'Ebed said, Who is Abimelech, and who is Shechem, that we should serve him? is not he the son of Yerubba'al? and Zebul his superintendent? serve the men of Chamor the father of Shechem; for why indeed should we serve him?
Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
29 And O that some one would put this people into my power! and I would remove Abimelech. And he let it be said to Abimelech, Increase thy army, and come out.
Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
30 And when Zebul the ruler of the city heard the words of Ga'al the son of 'Ebed, his anger was kindled.
Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
31 And he sent messengers unto Abimelech privately, saying, Behold, Ga'al the son of 'Ebed and his brothers are come to Shechem; and, behold, they incite the city to enmity against thee.
Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
32 And now rise up by night, thou and the people that are with thee, and lie in wait in the field:
Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
33 And it shall be, in the morning, the moment the sun shineth, that thou shalt rise early, and set upon the city; and, behold, when he and the people that are with him come out against thee, then mayest thou do to him as thy means may let thee.
Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
34 And Abimelech rose up, and all the people that were with him, by night, and they lay in wait against Shechem in four companies.
Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
35 And Ga'al the son of 'Ebed went out, and stood in the entrance of the city-gate: and Abimelech rose up, and the people that were with him, from the ambush.
Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
36 And when Ga'al saw the people, he said to Zebul, Behold, people are coming down from the tops of the mountains. And Zebul said unto him, Thou regardest the shadow of the mountains as men.
Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
37 And Ga'al spoke again and said, See people are coming down from the highest point of the land, and one company is coming along by the way of the grove of Me'onenim.
Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
38 Then said Zebul unto him, Where is now thy mouth, wherewith thou saidst, Who is Abimelech, that we should serve him! is not this the people that thou hast despised? go out now, I pray, and fight with them.
Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
39 And Ga'al went out before the men of Shechem, and fought with Abimelech.
Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
40 And Abimelech pursued him, and he fled before him, and many fell slain, even as far as the entrance of the gate.
Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
41 And Abimelech remained at Arumah: and Zebul banished Ga'al and his brothers, that they should not remain in Shechem.
Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
42 And it came to pass on the morrow, that the people went out into the field; and it was told to Abimelech.
Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
43 And he took the people, and divided them into three companies, and lay in wait in the field; and as he saw, and, behold, that the people were coming forth out of the city, he rose up against them, and smote them.
Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
44 And Abimelech, and the companies that were with him, spread forward, and took position in the entrance of the city-gate: and the two other companies spread over all that were in the fields, and smote them.
Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
45 And Ahimelech fought against the city all that day; and he captured the city, and the people that were therein he slew; and he beat down the city, and sowed it with salt.
Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
46 And when all the men of the tower of Shechem heard this, they entered into the stronghold of the house of the god Berith.
Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
47 And it was told unto Abimelech, that all the men of the tower of Shechem were gathered together.
Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
48 And Abimelech went thereupon up to mount Zalmon, he and all the people that were with him; and Abimelech took an axe in his hand, and cut down a bough from a tree, and bore it, and laid it on his shoulder; and he said unto the people that were with him, What ye have seen that I have done, make haste, and do like me.
Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
49 And all the people also cut down every man his bough, and followed Abimelech, and put the same to the stronghold, and set the stronghold over them on fire: and thus died also all the people of the tower of Shechem, about a thousand men and women.
Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
50 And Abimelech went then to Thebez, and encamped against Thebez, and captured it.
Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
51 But there was a strong tower within the city, and thither fled all the men and the women, and all the chief persons of the city, and shut the doors behind them, and went up to the roof of the tower.
Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
52 And Abimelech came up to the tower, and fought against it, and approached as far as the door of the tower to burn it with fire.
Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
53 But a certain woman cast a piece of an upper millstone upon Abimelech's head, and crushed his skull.
Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
54 Then called he hastily unto the young man that bore his armor, and said unto him, Draw thy sword, and slay me, that people may not say of me, A woman hath slain him. And his young man thrust him through, and he died.
Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
55 And when the men of Israel saw that Abimelech was dead, they departed every man to his place.
Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
56 Thus did God compensate the evil of Abimelech, which he had done unto his father, in slaying his seventy brothers:
Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
57 And all the evil of the men of Shechem did God bring back upon their own head; and there came upon them the curse of Yotham the son of Yerubba'al.
Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.

< Judges 9 >