< Judges 15 >
1 And it came to pass after some time, in the time of wheat-harvest, that Samson visited his wife with a kid; and he said, Let me go in to my wife into the chamber; but her father would not suffer him to go in.
Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
2 And her father said, I verily thought that thou didst utterly hate her; therefore I gave her to thy companion: is not her younger sister fairer than she? Let her be thine, I pray thee, instead of her.
Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
3 And Samson said to them, Now shall I be more blameless than the Philistines, though I do them evil.
Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
4 And Samson went and caught three hundred foxes, and took torches, and turned tail to tail, and put one torch between two tails in the midst;
Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
5 And he set the torches on fire, and let them go into the standing corn of the Philistines, and burnt up both shocks and standing corn, as also olive-yards.
Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
6 Then said the Philistines, Who hath done this! And they answered, Samson, the son-in-law of the Thimnite, because he hath taken his wife, and given her to his companion. And the Philistines went up, and burnt her and her father with fire.
Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
7 And Samson said unto them, Since ye will do the like of this, I will surely be avenged on you, and after that will I cease.
Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
8 And he smote them hip and thigh with a great slaughter; and he went down and tarried in the cleft of the rock 'Etam.
Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
9 And the Philistines went up, and encamped in Judah, and spread themselves in Lechi.
Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
10 And the men of Judah said, Why are ye come up against us? And they answered, To bind Samson are we come up, to do to him as he hath done to us.
Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
11 Thereupon went three thousand men of Judah down to the cleft of the rock 'Etam, and said to Samson, Knowest thou not that the Philistines rule over us? and what is this that thou hast done unto us? And he said unto them, As they did unto me, so have I done unto them.
Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
12 And they said unto him, To bind thee are we come down, to deliver thee into the hand of the Philistines. And Samson said unto them, Swear unto me, that ye will not assail me yourselves.
Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
13 And they said unto him, thus, No; for we will [only] bind thee fast, and deliver thee into their hand; but we will in no-wise kill thee. And they bound him with two new cords, and brought him up from the rock.
Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
14 When he was come unto Lechi, the Philistines shouted against him; but the Spirit of the Lord came suddenly over him, and the cords that were upon his arms became as flax threads that are burnt with fire, and his bands melted from off his hands.
Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
15 And he found a fresh jaw-bone of an ass, and put forth his hand, and took it, and smote therewith a thousand men.
Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
16 And Samson said, With a jaw-bone of an ass, heaps upon heaps, with the jaw-bone of an ass have I smitten a thousand men.
Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
17 And it came to pass, when he had made an end of speaking, that he cast away the jaw-bone out of his hand, and called that place Ramath-lechi.
Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
18 And he became very thirsty, and he called on the Lord, and said, Thou hast granted through the hand of thy servant this great deliverance; and now shall I die for thirst, and fall into the hand of the uncircumcised?
Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
19 But God clave a hollow place that was at Lechi, and there came forth water out of it; and he drank, and his spirit came again, and he revived; wherefore he called the name thereof 'En-hakkore, which is in Lechi unto this day.
Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
20 And he judged Israel in the days of the Philistines twenty years.
Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.