< Joshua 7 >

1 But the children of Israel committed a trespass on the devoted things; for 'Achan, the son of Carmi, the son of Zabdi, the son of Zerach, of the tribe of Judah, took of the devoted things: and the anger of the Lord was kindled against the children of Israel.
Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
2 And Joshua sent men from Jericho to 'Ai, which is beside Beth-aven, on the east side of Beth-el, and said unto them, thus, Go up and spy out the country. And the men went up and spied out 'Ai.
Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
3 And they returned to Joshua, and said unto him, Let not all the people go up; but let about two or three thousand men go up and smite 'Ai: do not fatigue all the people [to go] thither; for they are but few.
Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
4 So there went up thither of the people about three thousand men; and they fled before the men of 'Ai.
Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
5 And the men of 'Ai smote of them about thirty and six men; and they chased them from before the gate unto the stone-quarries, and smote them on the declivity [of the hill]; wherefore the heart of the people melted, and became as water.
Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
6 And Joshua rent his clothes, and fell upon his face to the earth before the ark of the Lord until the evening, he with the elders of Israel, and they put dust upon their head.
Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
7 And Joshua said, Alas, O Lord Eternal, wherefore hast thou caused this people to pass over the Jordan, to deliver us into the hand of the Emorites, to destroy us? and oh! that we had been content, and dwelt on the other side of the Jordan!
Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
8 I pray thee, O Lord, what shall I say, since Israel have turned their back before their enemies!
Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
9 And when the Canaanites and all the inhabitants of the land will hear of it, they will environ us round, and cut off our name from the earth; and what wilt thou do for thy great name?
Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
10 And the Lord said unto Joshua, Get thee up; wherefore liest thou upon thy face.
Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
11 Israel hath sinned, and they have also transgressed my covenant which I have commanded them; and they have also taken of the devoted things, and have also stolen, and have also dissembled, and they have also put it into their own vessels.
Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
12 Therefore will the children of Israel not be able to stand up before their enemies; their back will they turn before their enemies, because they have become accursed: I will not be any more with you, except ye destroy the accursed from among you.
Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
13 Rise up, sanctify the people, and say, Sanctify yourselves against tomorrow; for thus hath said the Lord the God of Israel, An accursed thing is in the midst of thee, O Israel: thou shalt not be able to stand up before thy enemies, until ye have removed the accursed from among you.
“Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
14 And ye shall be brought near in the morning according to your tribes: and it shall be, that the tribe which the Lord will seize shall come near according to its families; and the family which the Lord will seize shall come near by households; and the household which the Lord shall seize will come near by its men.
“Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
15 And it shall be, that he that is seized with the accursed thing shall be burnt with fire, he, and all that he hath; because he hath transgressed the covenant of the Lord, and because he hath wrought wickedness in Israel.
Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
16 So Joshua rose up early in the morning, and brought Israel near by their tribes, and the tribe of Judah was seized;
Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
17 And he brought near the family of Judah, and he seized the family of the Zarchites; and he brought near the family of the Zarchites by its men, and Zabdi was seized;
Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
18 And he brought near his household by its men, and 'Achan, the son of Carmi, the son of Zabdi, the son of Zerach, of the tribe of Judah, was seized.
Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
19 And Joshua said unto 'Achan, My son, give, I pray thee, glory to the Lord, the God of Israel, and make confession unto him; and tell me, I pray thee, what thou hast done: hide nothing from me.
Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
20 And 'Achan answered Joshua, and said, Truly! I have indeed sinned against the Lord the God of Israel, and thus and thus have I done:
Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
21 I saw among the spoil a handsome Babylonish mantle, and two hundred shekels of silver, and a wedge of gold of fifty shekels in weight, and I coveted them, and took them; and, behold, they are hidden in the earth in the midst of my tent, with the silver beneath the same.
Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
22 Joshua thereupon sent messengers, and they ran unto the tent; and, behold, it was hidden in his tent, and the silver beneath it.
Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
23 And they took them out of the midst of the tent, and brought them unto Joshua, and unto all the children of Israel, and they laid them out before the Lord.
Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
24 And Joshua took 'Achan the son of Zerach, and the silver, and the mantle, and the wedge of gold, and his sons, and his daughters, and his ox, and his ass, and his sheep, and his tent, and all that he had, and all Israel were with him, and they brought them up unto the valley of 'Achor.
Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
25 And Joshua said, How hast thou troubled us! so shall the Lord trouble thee this day. And all Israel stoned him with stones, and burnt them with fire, after they had stoned them with stones.
Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
26 And they raised over him a great heap of stones [which is] unto this day; and the Lord turned from the fierceness of his anger. Wherefore the name of that place was called, The valley of 'Achor, unto this day.
Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.

< Joshua 7 >