< Job 5 >
1 Do but call: is there one that will answer thee? and to whom of the saints wilt thou turn thyself?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 For vexation will prove death to a foolish man, and jealousy will slay the simple.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 I have myself seen the foolish taking root; but I suddenly held his habitation as accursed.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 His children are far from help, and men crush them in the gate, with no one to deliver them.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 [He it is] whose harvest the hungry eateth up, and taketh it even out of the thorns, and the robber snatcheth eagerly after their substance.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 For wrong doth not come forth out of the dust, neither doth trouble grow up out of the ground;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 But man is born unto trouble, as young birds take up their flight.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 I, however, would have besought God, and unto God would I have committed my cause;
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Who doth great things which are unsearchable, marvelous things till they are without number;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Who giveth rain upon the surface of the earth, and sendeth out waters over the face of the fields;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 To set up the lowly on high, that those who mourn may rise high to happiness;
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 [But] who frustrateth the plans of the crafty, so that their hands cannot execute their well-devised counsel;
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Who catcheth the wise in their own craftiness; and the advise of the perverse is hastened on headlong;
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 By day they meet with darkness, and as though it were night they grope about in the noon of day;
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 But who saveth from the sword, from their mouth, and from the hand of the mighty, the needy one:
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 And so cometh to the indigent hope, and iniquity stoppeth her mouth.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Behold, happy is the man whom God admonisheth: despise then not the correction of the Almighty.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 For he it is that woundeth, and bindeth up: he smiteth, and his hands do heal.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 In six distresses will he deliver thee; and in seven there shall no evil touch thee.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 In famine he redeemeth thee from death; and in war from the power of the sword.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Against the scourge of the tongue shall thou he hidden; and thou needest not be afraid of destruction when it cometh.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 At destruction and famine canst thou laugh; and thou needest not have any fear of the beasts of the earth.
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 For with the stones of the field shalt thou have thy covenant; and the beasts of the field shall be at peace with thee.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 And thou shalt know that there is peace in thy tent; and thou wilt look over thy habitation, and shalt miss nothing.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 And thou shalt know that thy seed is numerous, and thy offspring as the herbage of the earth.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Thon wilt go in a ripe age unto the grave, as a shock of corn is carried home in its season.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Behold this, we have searched it out, so it is: hear it, and do thou note it well for thyself.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”