< Job 39 >
1 Knowest thou the time when the chamois of the rock bring forth? or markest thou when the hinds do calve?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Numberest thou the months of gestation which they complete and knowest thou the time when they bring forth?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 They bend themselves: they drop their young ones; throw off their pains.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Their little ones become strong; they grow up in the open field; they go forth, and return not unto them.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Who sent out the wild ass free? or who loosened the bonds of the forest-ass?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 To whom I assigned the wilderness as his house, and the salty land as his dwellings.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 He laugheth at the noise of a town, and the shoutings of the driver he heareth not.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 What he espieth on the mountains is his pasture, and after every green thing doth he search.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Will the forest-ox be willing to serve thee, or will he stay over night at thy crib?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Canst thou bind the forest-ox with a rope [to labor] in the furrow? or will he harrow valleys, following after thee?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Wilt thou trust him, because his strength is great? and wilt thou leave to him thy labor?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Wilt thou confide in him, that he should bring home thy seed, and gather it into thy threshing-floor?—
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 The wing of the ostrich moveth joyfully: hath she the pinions and plumage of the careful stork?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 [No, ] for she intrusteth her eggs to the earth, and letteth them be hatched out on the dust:
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 And she forgetteth that a foot may crush them, or that the beast of the field may stamp them down.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 He hath made her callous against her young, as though they were not hers: her labor is in vain, [but she feeleth] no dread;
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Because God hath denied her wisdom, and he hath not imparted to her understanding.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 At the time she raiseth herself up on high, she laugheth at the horse and his rider.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Dost thou give the horse strength? dost thou clothe his neck with the rolling mane?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Canst thou make him jump like a locust? his majestic snort is terrible.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Men spy about in the valley, and he rejoiceth in his strength: he goeth forth to meet the armed array.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 He laugheth at fear, and is not dismayed; and turneth not back from before the sword.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Over him rattle the quiver, the glittering spear and the lance.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 With impatient noise and rage he holloweth [with his hoof] the ground, and keepeth not quiet when the cornet's voice [is heard].
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Midst the sound of the cornet he uttereth his joyful neigh; and from afar he perceiveth the battle, the loud call of the captains, and the battle-cry.—
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Is it through thy understanding that the hawk flieth along, and spreadeth out his wings toward the south?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Or is it by your order that the eagle doth mount upward, and buildeth high up his nest?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 On a rock he dwelleth, and spendeth his nights, on a rocky crag and mountain fastness.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 From there he espieth his food, from afar can his eyes behold.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 His young ones, also, sip up blood: and where the slain be, there is he.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”