< Job 3 >
1 After this time Job opened his mouth, and cursed his day.
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 And Job commenced, and said,
Ndipo Yobu anati:
3 Oh that the day whereon I was born might perish, and the night when it was said, There hath been a male child conceived.
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 May that day be [covered with] darkness; may not God from above inquire for it, and may no light beam upon it.
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Oh that darkness and the shadow of death might defile it; may a cloud rest upon it; may the blackness of the day terrify it.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 Yon night — let darkness seize upon it; let it not be united to the days of the year; let it not come into the number of the [periods lighted by the] moon.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 Lo, may that night be solitary, let no song of joy occur thereon.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Let those denounce it that curse the day, who are ready to raise up their mourning cry.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Let the stars of its twilight be darkened; let it hope for light, and there be none; and let it not behold the eyelids of the morning-dawn;
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Because God closed not against me the doors of the womb, and thus concealed trouble from my eyes.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Why did I not die [the moment I issued] from the womb, and [why] was I not born merely to perish at once?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Wherefore were knees ready to receive me? and for what purpose were breasts there that I might suck?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 For now should I be lying still and be quiet; I should sleep: then would I be at rest,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 With kings and counsellors of the earth, who build up ruined places for themselves;
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 Or with princes possessing gold, who fill their houses with silver;
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Or as an untimely birth, hidden [from view] I should not exist; as infants that never have seen the light;
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 There [where] the wicked cease from troubling; and where the exhausted weary are at rest;
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 [Where] the prisoners repose together, [and] they hear no more the taskmaster's voice.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 The small with the great is there, and the servant free from his master.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Wherefore giveth He now light to the labor-laden, and life unto the bitter in soul?
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 Who wait for death, which [cometh] not; and who dig for it sooner than for hidden treasures;
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 Who would rejoice even to exulting, who would be glad could they but find a grave?
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 [Why is light given] to a man whose way is hidden, and around whom God hath placed a fence?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 For before my food cometh my groaning, and like the water are poured forth my loud complaints.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Because what I greatly dreaded is come upon me, and what I apprehended is come unto me.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 I have had no safety, and no quiet, and no rest; and [now] harrowing trouble is come.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”