< Job 23 >
1 Then answered Job, and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Even now is my complaint bitter: my suffering is heavier than my groans.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 Oh who would grant that I knew where I might find him! that I might attain to his Judgment throne!
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 I would put in order before him my cause, and my mouth would I fill with arguments.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 I should know the words which he might answer me, and understand what he might say unto me.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 Would he with his power contend against me? he would truly not lay such doings to my charge.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 There would an upright one argue with him; and I should be allowed to escape for ever by my judge.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 But, lo, I go eastward—and he is not there; and to the west— and I cannot perceive him;
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 When he doth great things at the north, I behold him not; he hideth himself in the south—and I see him not.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 But he knoweth the way that I take: were he to probe me, I should come forth as gold.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 On his steps my foot hath held fast: his way have I kept, and swerved not.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 From the commandment of his lips have I also not moved away: as a fixed statute for me have I treasured up the sayings of his mouth.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 But he is unchangeably one, and who can turn him? And what his will desireth, even that he doth.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 For he will bring to completion what hath been destined for me: and like these hath he many other things with him.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Therefore am I terrified at his presence: I will reflect, and be in dread of him.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 Still God hath made timid my heart, and the Almighty hath terrified me;
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 Because I was not destroyed before this darkness, and because he hath not hidden from my face [this] gloom.
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.