< Jeremiah 41 >

1 Now it came to pass in the seventh month, that Ishmael the son of Nethanyah the son of Elishama', of the royal seed, and the chiefs of the king, even ten men with him, came unto Gedalyahu the son of Achikam to Mizpah; and they ate there bread together in Mizpah.
Pa mwezi wachisanu ndi chiwiri Ismaeli mwana wa Netaniya, mdzukulu wa Elisama amene anali wa banja laufumu ndiponso mmodzi wa atsogoleri a ankhondo a mfumu, anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ndi anthu khumi. Pamene ankadya naye kumeneko,
2 Then arose Ishmael the son of Nethanyah, and the ten men that were with him, and smote Gedalyahu the son of Achikam the son of Shaphan with the sword, and put to death him, whom the king of Babylon had appointed governor over the land.
Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu khumi aja anayimirira ndi kupha ndi lupanga Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani. Choncho anapha munthu amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.
3 And all the Jews that were with him, even with Gedalyahu, at Mizpah, and the Chaldeans that were found there, even the men of war, did Ishmael slay.
Ismaeli anaphanso Ayuda onse amene anali pamodzi ndi Gedaliya ku Mizipa, kuphatikizanso asilikali a Ababuloni amene anali ku Mizipako.
4 And it came to pass on the second day after he had put Gedalyahu to death, while no man knew of it,
Mmawa mwake, anthu asanadziwe kuti Gedaliya waphedwa,
5 That there came certain men from Shechem, from Shiloh, and from Samaria, eighty men [in all], having their beards shaven, and their clothes rent, and having cut themselves, with meat-offerings and frankincense in their hand, to bring the same to the house of the Lord.
kunafika anthu 80 ochekera ku Sekemu, Silo ndi Samariya, amene anali atameta ndevu zawo, atangʼamba zovala zawo ndi kudzichekacheka. Iwowa anatenga chopereka cha ufa ndi lubani kuti adzapereke ku Nyumba ya Yehova.
6 And Ishmael the son of Nethanyah went forth from Mizpah to meet them, going along and weeping: and it came to pass as he met them, that he said unto them, Come to Gedalyahu the son of Achikam.
Ismaeli mwana wa Netaniya anachoka ku Mizipa akulira kupita kukakumana nawo. Atakumana nawo, iye anati, “Bwerani mudzaonane ndi Gedaliya mwana wa Ahikamu.”
7 And it happened, as they entered into the midst of the city, that Ishmael the son of Nethanyah slaughtered them, [and cast them] into the midst of the cistern, he, and the men that were with him.
Atafika pakati pa mzinda, Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu amene anali naye anawapha anthuwo ndi kuwaponya mʼchitsime.
8 But ten men were found among them that said unto Ishmael, Slay us not; for we have some things hidden in the field, [such as] wheat, and barley, and oil, and honey. So he forbore, and slew them not in the midst of their brethren.
Koma anthu khumi a gululo anawuza Ismaeli kuti, “Musatiphe! Tili ndi tirigu ndi barele, mafuta ndi uchi, zimene tabisa mʼmunda.” Choncho anawasiya ndipo sanawaphere pamodzi ndi anzawo aja.
9 And the cistern wherein Ishmael cast all the corpses of the men, whom he had slain in company with Gedalyahu, is the same which king Assa had made on account of Ba'sha the king of Israel: this did Ishmael the son of Nethanyah fill with slain persons.
Tsono chitsime chimene anaponyamo mitembo ya anthu amene anawaphawo pamodzi ndi mtembo wa Gedaliya chinali chimene mfumu Asa anachikumba poopsedwa ndi Baasa mfumu ya Israeli. Ismaeli mwana wa Netaliya anachidzaza ndi mitembo.
10 Then did Ishmael carry away captive all the residue of the people that were in Mizpah, the king's daughters, and all the people that were remaining in Mizpah, whom Nebuzaradan the captain of the guard had entrusted to Gedalyahu the son of Achikam: and Ishmael the son of Nethanyah carried them away captive, and went off to pass over to the children of Ammon.
Pambuyo pake Ismaeli anatenga ukapolo anthu ena onse amene anali ku Mizipa: ana aakazi a mfumu pamodzi ndi ena onse amene anatsalira kumeneko, amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anapatsa Gedaliya mwana wa Ahikamu kuti akhale bwanamkubwa wawo. Ismaeli mwana wa Netaliya anatenga ukapolo anthuwa ndi kuwoloka nawo kumapita ku dziko la Aamoni.
11 But when Jochanan the son of Kareach, and all the captains of the armies that were with him, heard of all the evil that Ishmael the son of Nethanyah had done:
Pamene Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye pamodzi anamva zoyipa zonse zimene Ismaeli mwana wa Netaniya anachita,
12 Then did they take all the men, and went to fight with Ishmael the son of Nethanyah, and found him by the great water[-pool] that is near Gib'on.
anatenga ankhondo awo onse kupita kukamenyana ndi Ismaeli mwana wa Netaniya. Anakamupeza kufupi ndi chidziwe chachikulu cha ku Gibiyoni.
13 And it came to pass, when all the people who were with Ishmael saw Jochanan the son of Kareach, and all the captains of the armies that were with him, that they were rejoiced.
Pamene anthu onse amene Ismaeli anawagwira anaona Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali naye, anasangalala.
14 And all the people that Ishmael had carried away captive from Mizpah turned about and returned, and went unto Jochanan the son of Kareach.
Anthu onse amene Ismaeli anawagwira ukapolo ku Mizipa anabwerera ndi kupita kwa Yohanani mwana wa Kareya.
15 But Ishmael the son of Nethanyah escaped with eight men from the presence of Jochanan, and he went to the children of 'Ammon.
Koma Ismaeli pamodzi ndi anthu ake asanu ndi atatu, anathawa Yohanani ndi kuthawira kwa Aamoni.
16 Then took Jochanan the son of Kareach, and all the captains of the armies that were with him, all the remnant of the people whom he had recovered from Ishmael the son of Nethanyah, from Mizpah, after he had slain Gedalyah the son of Achikam, the adult males, the men of war, and the women, and the children, and the eunuchs, whom he had brought back from Gib'on;
Kenaka Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye anatsogolera anthu onse otsala a ku Mizipa amene anawapulumutsa kwa Ismaeli mwana wa Netaniya atapha Gedaliya mwana wa Ahikamu. Anthu amenewa anali: asilikali, akazi, ana ndi amuna ofulidwa otumikira mfumu amene anawatenga ku Gibiyoni.
17 And they went, and remained in Geruth-Kimham, which is by Beth-lechem, to go to enter into Egypt,
Ndipo ananyamuka nayima ku Geruti Kimuhamu pafupi ndi Betelehemu pa ulendo wawo wopita ku Igupto
18 Because of the Chaldeans; for they were afraid of them; because Ishmael the son of Nethanyah had slain Gedalyahu the son of Achikam, whom the king of Babylon had appointed governor over the land.
kuthawa Ababuloni. Iwo anaopa Ababuloniwo chifukwa Ismaeli mwana wa Netaniya anapha Gedaliya mwana wa Ahikamu, amene mfumu ya ku Babuloni inamuyika kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.

< Jeremiah 41 >