< Isaiah 7 >

1 And it came to pass in the days of Achaz the son of Jotham, the son of 'Uzziyahu, the king of Judah, that Rezin the king of Syria, and Pekach the son of Remalyahu, the king of Israel, went up toward Jerusalem to war against it; but were not able to make an attack upon it.
Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
2 And it was told unto the house of David, saying, Syria is encamped with Ephraim; and his heart trembled, with the heart of his people, as the trees of the forest are shaken before the wind.
Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
3 And the Lord said unto Isaiah, Go forth now to meet Achaz, thou with Shear-yashub thy son, to the end of the aqueduct of the upper pool, on the highway of the washer's field;
Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
4 And thou shalt say unto him, Take heed, and be quiet; fear not, and let thy heart not become faint because of these two stumps of smoking firebrands, before the fierce anger of Rezin with Syria, and of the son of Remalyahu.
Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
5 Forasmuch as Syria, [with] Ephraim and the son of Remalyahu, have taken evil counsel against thee, saying,
Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
6 Let us go up against Judah, and besiege it, and let us make a breach therein for us, and set up as king in the midst of it the son of Tabeal:
‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
7 Thus hath said the Lord Eternal, It shall not succeed, and it shall not come to pass.
Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
8 For the head of Syria is Damascus, and the head of Damascus is Rezin: and within sixty and five years shall Ephraim be broken, to be no more a people.
pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
9 And the head of Ephraim is Samaria, and the head of Samaria is Remalyahu's son. If ye will not believe, surely ye shall not have permanence.
Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
10 And the Lord continued to speak unto Achaz, saying,
Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
11 Ask thee a sign from the Lord thy God; ask it in the depth, or high up above. (Sheol h7585)
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
12 But Achaz said, I will not ask, and I will not tempt the Lord.
Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
13 And he said, Hear ye now, O house of David! Is it too little for you to weary men, that ye will weary also my God?
Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
14 Therefore will the Lord himself give you a sign: behold, this young woman shall conceive, and bear a son, and she shall call his name 'Immanu-el, [God with us].
Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
15 Cream and honey shall he eat, so soon as he knoweth to refuse the evil, and to choose the good.
Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
16 For before yet the child shall know to refuse the evil, and to choose the good, shall be forsaken the land, of the kings of which thou feelest dread.
Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
17 The Lord will bring over thee, and over thy people, and over thy father's house, days that have not come, from the day that Ephraim withdrew from Judah, —the king of Assyria.
Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
18 And it shall come to pass on that day, that the Lord will call for the fly that is in the uttermost end of the streams of Egypt, and for the bee that is in the land of Assyria.
Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
19 And they shall come, and shall encamp, all of them, in the desolate valleys, and in the clefts of the rocks, and upon all thorn-hedges, and upon all bushes.
Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
20 On the same day will the Lord shave with the razor that is hired, from among those on the other side of the river, with the king of Assyria, the head, and the hair of the feet: and also the beard shall it entirely remove.
Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
21 And it shall come to pass on that day, that a man shall nourish [but] one young cow, and two sheep;
Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
22 And it shall happen, that for the abundance of milk which they shall give he shall eat cream; for cream and honey shall eat every one that is left in the midst of the land.
Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
23 And it shall come to pass on that day, that every place, where there are [now] a thousand vines worth a thousand silver shekels, shall be, —yea, this shall be [given up] to briers and thorns.
Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
24 With arrows and with bows shall men enter thither; because all the land shall become [covered with] briers and thorns.
Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
25 And all mountains that are worked with the mattock, there shall not come thither the fear of briers and thorns: and they shall serve for the pasture of oxen, and for the treading of sheep.
Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.

< Isaiah 7 >