< Isaiah 55 >

1 Ho, every one of ye that thirsteth, come ye to the water, and he too that hath no money: come ye, buy, and eat; yea, come, buy without money and without price wine and milk.
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Wherefore will ye spend money for what is not bread? and your labor for what satisfieth not? hearken then unto me, and eat what is good, and let your soul delight itself in fatness.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Incline your ear, and come unto me, hear, and your soul shall live; and I will make with you an everlasting covenant, the promised mercies of David, which are sure.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Behold, for a lawgiver unto the people have I appointed him, a prince and commander to the people.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Behold, a nation thou knowest not shalt thou call, and a nation that knew thee not shall run unto thee; for the sake of the Lord thy God, and for the Holy One of Israel, for he hath glorified thee.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Seek ye the Lord, while he may be found, call ye on him, while he is near.
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Let the wicked forsake his way, and the man of unrighteousness his thoughts; and let him return unto the Lord, and he will have mercy upon him, and unto our God, for he will abundantly pardon.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 For not my thoughts are your thoughts, and not your ways are my ways, saith the Lord.
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 For as high as the heavens are above the earth, so high are my ways above your ways, and my thoughts above your thoughts.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 For as the rain and the snow come down from heaven, and return not thither, but water the earth, and render it fruitful, and cause it to bring forth plants; and give seed to the sower and bread to him that eateth:
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 So shall ever be my word which goeth forth from my mouth, it shall not return unto me without effect; but it accomplisheth what I desire, and it prospereth in that whereto I have sent it.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 For in joy shall ye go out, and in peace shall ye be brought home: the mountains and the hills shall break forth before you into song, and all the trees of the field shall clap their hands.
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Instead of the thorn shall come up the fir-tree, and instead of the nettle shall come up the myrtle; and it shall be unto the Lord for a name, for a sign of everlasting that shall not be cut off.
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”

< Isaiah 55 >