< Isaiah 45 >
1 Thus hath said the Lord to his anointed, to Cyrus, whom I have taken hold of by his right hand, to subdue nations before him, even the loins of kings will I ungird, to open before him [city-]doors, and gates that they shall not be shut;
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 I myself will go before thee, and proud eminences will I level: doors of brass will I break in pieces, and bolts of iron will I cut asunder.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 And I will give unto thee the treasures of darkness, and riches hidden in secret places; in order that thou mayest know that I am the Lord, who call thee by thy name, the God of Israel;
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 For the sake of my servant Jacob, and Israel my elect; and I have called thee by thy name: I have designated thee, though thou hast not known me.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 I am the Lord, and there is none else, beside me there is no god; I assisted thee, though thou hast not known me.
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 In order that they may know from the rising of the sun, and from its setting, that there is nothing without me. I am the Lord, and there is no one else;
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Forming the light, and creating darkness; making peace, and creating evil: I the Lord do all these things.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Drop down ye heavens, and let the skies distil blessing; let the earth open and let them [all] be fruitful of prosperity, and let righteousness spring up likewise: I the Lord have created it.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Woe unto him that contendeth with the one who formed him—a potsherd among the potsherds of the earth. Shall the clay say to him that fashioneth it, What makest thou? or thy work, He hath no hands?
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Woe unto him that saith unto [his] father, What begettest thou? or to the woman, What bringest thou forth?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Thus hath said the Lord, the Holy One of Israel, and he who hath formed him, About events to come will you ask me? concerning my sons, and concerning the work of my hands will ye command me?
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 [When] I myself have made the earth, and created man upon it; [when] I, even my hands, have stretched out the heavens, and I have ordained all their host.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 I myself have waked him up in righteousness, and all his ways will I make straight: he shall build my city, and my exiles shall he dismiss free, not for purchase-money nor for presents, saith the Lord of hosts.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Thus hath said the Lord, The labor of Egypt, and the merchandise of Ethiopia, and of the Sabeans, men of high stature, shall pass over unto thee, and thine shall they be: behind thee shall they walk; in chains shall they pass along, and unto thee shall they bow, unto thee shall they pray, [saying] Yea, only among thee is God; and there is no one else beside God.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Verily thou art a God that hidest thyself, O God of Israel, the Saviour.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 They are ashamed, and also confounded, all of them: together shall they go to confusion that are makers of idols.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 [But] Israel shall be helped by the Lord with an everlasting salvation: ye shall not be ashamed and not be confounded unto all eternity.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 For thus hath said the Lord the creator of the heavens; he, the God that formed the earth and made it; he that hath established it, —not for naught did he create it, to be inhabited did he form it: I am the Lord; and there is no one else.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Not on a secret spot have I spoken, in a dark place of the earth; I said not unto the seed of Jacob, Seek ye me for naught; [but] I the Lord speak righteousness, I declare things that are right.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Assemble yourselves and come; draw near together, ye escaped fugitives of the nations! They have no knowledge that carry the wood of their graven image, and pray unto a god that cannot save.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Tell ye, and bring them near; yea, let them take counsel together: Who hath announced this in ancient times? told it from the beginning? is it not I the Lord? and there is no other god without me, a just god and a saviour; there is none beside me.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Turn unto me, so that ye may be helped, all ye ends of the earth; for I am God, and there is no one else.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 By myself have I sworn, righteousness is gone out of my mouth, a word [which] shall not return, That unto me every knee shall bend, every tongue shall swear.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Only in the Lord, —shall men say of me, —there are righteousness and strength. Unto him shall come and be ashamed all that are incensed against him.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 In the Lord shall be justified, and shall glory themselves all the seed of Israel.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.