< Isaiah 27 >
1 On that day will the Lord punish with his heavy and great and strong sword leviathan the flying serpent, and leviathan the crooked servant; and he will slay the crocodile that is in the sea.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 On that day sing ye a song of the vineyard of excellent wine.
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 “I the Lord do keep it; every moment will I water it: that no one shall hurt it, night and day will I keep it.
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 Wrath have I not: who would set the briers and thorns against me in battle? I would pass through them, and I would burn them altogether.
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 If he but take hold of my strength, make peace with me; make peace with me.”
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 In the future shall Jacob yet take root; Israel shall bud and blossom, and shall fill the face of the world with fruit.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Hath he smitten him, as he smote the one that smote him? or was he slain with the same slaughter as those of him that were slain?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 In measure, by driving him forth, thou strivest with him: he removed him with his violent storm on the day of the east wind.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 Therefore by this [only] shall the iniquity of Jacob be atoned; and this shall be all the fruit of the taking away of his sin; when he maketh all the stones of the altar as limestones that are beaten in pieces, when there shall not arise again any groves and sun-images.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 For [by this] the fortified city shall be desolate, the habitation be forsaken, and left like a wilderness; there shall the calf feed, and there shall it lie down, and consume its branches.
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 When its boughs are withered, they shall be broken off; women will come and set them on fire; for it is not a people of understanding; therefore he that made it will not have mercy on it, and he that formed it will show it no favor.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 And it shall come to pass on that day, that the Lord will beat off [the fruit] from the channel of the River up to the brook of Egypt; but ye shall be gathered up one by one, ye children of Israel.
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 And it shall come to pass on that day, that the great cornet shall be blown, and then shall come those who are lost in the land of Asshur, and those who are outcasts in the land of Egypt, and they shall prostrate themselves before the Lord on the holy mount at Jerusalem.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.