< Hosea 7 >

1 Should I desire to heal Israel, then would the iniquity of Ephraim and the wickedness of Samaria be laid open; for they commit falsehood; and the thief entereth [secretly], and the troop of robbers is spread abroad without.
Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
2 And they never think in their own heart that I remember all their wickedness: though now their own doings are all round about them; before my face are they present.
Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
3 With their wickedness they make the king glad, and with their lies the princes.
“Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
4 They are all adulterers, as an oven well heated by the baker: [when] he that stirreth [the fire] resteth awhile from kneading the dough, until it be leavened.
Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
5 On the day of our king's [entering on his rule] the princes are made sick with the fumes of wine: [the king] joineth his hand with scorners.
Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
6 For they make ready their heart for their tricky deeds, like the oven, the baker whereof sleepeth all the night, while in the morning it gloweth as a flaming fire.
Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
7 They are all hot as an oven, they devour their judges; all their kings are fallen: there is none among them that calleth unto me.
Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
8 Ephraim mixeth himself indeed among the nations: Ephraim is a cake not turned.
“Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
9 Strangers devour his strength, and he knoweth it not: yea, gray hairs are sprinkled about on his [head], yet he knoweth not.
Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
10 And humbled was the pride of Israel before his own face; but they did not return to the Lord their God, and sought him not, notwithstanding all this.
Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
11 And Ephraim is become like a silly dove without understanding: Egypt did they call hither, to Assyria did they go.
“Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
12 As they go, so will I spread out my net over them; as the fowls of the heaven will I bring them down: I will chastise them, as it hath been announced to their congregation.
Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
13 Woe unto them! for they have fled from me; destruction shall come unto them, because they have transgressed against me: though I desired to redeem them, they yet spoke lies against me.
Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
14 And they cried not unto me with their heart, when they howled upon their beds: for corn and new wine they assemble themselves, and they rebel against me.
Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
15 And I desired to instruct and to strengthen their arms; yet would they devise evil against me.
Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
16 They never return upward: they are like a deceitful bow: by the sword shall their princes fall because of the rage of their tongue; this shall be their derision in the land of Egypt.
Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.

< Hosea 7 >