< Hosea 6 >

1 “Come, and let us return unto the Lord; for he hath torn, and he will heal us; he hath smitten, and he will bind up our wounds.
“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
2 He will revive us after two days: on the third day he will raise us up, and we shall live in his presence.
Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
3 And let us feel it, that we may strive to know the Lord; bright as the morning-dawn is his rising; and he will come as the rain unto us, as the latter rain that maketh fruitful the earth.”
Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
4 What shall I do unto thee, O Ephraim? what shall I do unto thee, O Judah? for your piety is as a morning cloud, and as the early dew that passeth away.
Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
5 Therefore did I hew [them] down by means of the prophets; I slew them by the words of my mouth: and thy punishments go forth like the light.
Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
6 For piety I desired, and not sacrifice; and the knowledge of God, more than burnt-offerings.
Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
7 But they, like an ordinary man, have transgressed the covenant: there have they dealt treacherously against me.
Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
8 Gil'ad is become a city of workers of wickedness, is full of traces of blood.
Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
9 And as troops that lie in wait for a man, so is the band of priests, they murder on the way in unison; for they commit scandalous deeds.
Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
10 On the house of Israel have I seen a horrible thing: there is lewdness in Ephraim, Israel is become defiled.
Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
11 Also for thee, O Judah, will a harvest be prepared, when I bring back the captivity of my people.
“Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”

< Hosea 6 >