< Hosea 12 >
1 Ephraim feedeth on wind, and pursueth the east wind; the whole day he increaseth deceit and corruption; and a covenant do they make with Assyria, and oil is carried into Egypt.
Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 But with Judah also hath the Lord [to hold] a controversy; and to punish Jacob according to his ways, according to his doings will he recompense him.
Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 In the womb he took his brother by the heel, and in his strength he strove with an angel.
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Yea, he strove with an angel, and prevailed; he wept, and made supplication unto him: in Beth-el he should find him, and there he will speak with us.
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
5 And the Lord God of hosts, the Eternal One is his memorial.
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Therefore do thou return to thy God: keep goodness and justice, and wait on thy God continually.
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 But like a merchant, who hath the balances of deceit in his hand, loving to overreach,
Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
8 Did Ephraim say, I am certainly become rich, I have acquired substance unto myself: it is all through my labors; they will find no iniquity in me, that could be sin.
Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 And I am the Lord thy God from the land of Egypt: I will yet make thee dwell in tents, as in the days of antiquity.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 And I have spoken through the prophets, and I myself have multiplied visions, and by the means of the prophets have I spoken in similitudes.
Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 If in Gil'ad there was misfortune, [it is because] there was naught but idolatry; in Gilgal they sacrificed bullocks [to idols]: their altars also are as stone-heaps on the furrows of the fields.
Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
12 And Jacob fled into the fields of Syria, and Israel served for a wife, and for a wife he kept [the flocks].
Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 And by a prophet did the Lord bring Israel out of Egypt, and by a prophet was he guarded.
Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 [Yet] Ephraim provoked [him] to anger most bitterly: therefore will his Lord cast his blood-guiltiness upon him, and his reproach will he recompense unto him.
Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.