+ Genesis 1 >

1 In the beginning God created the heaven and the earth.
Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 And the earth was without form and void, and darkness was upon the face of the deep; and the spirit of God was waving over the face of the waters.
Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
3 And God said, Let there be light; and there was light.
Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
4 And God saw the light that it was good; and God divided between the light and the darkness.
Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
5 And God called the light Day, and the darkness he called Night. And it was evening and it was morning, the first day.
Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
6 And God said, Let there be an expansion in the midst of the waters, and let it divide between waters and waters.
Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
7 And God made the expansion, and divided between the waters which were under the expansion and the waters which were above the expansion: and it was so.
Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
8 And God called the expansion Heaven. And it was evening and it was morning, the second day.
Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
9 And God said, Let the waters under the heaven be gathered together unto one place, and let the dry land be visible: and it was so.
Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
10 And God called the dry land Earth; and the gathering together of the waters he called Seas: and God saw that it was good.
Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
11 And God said, Let the earth bring forth grass, herbs yielding seed, fruit-trees yielding fruit after their kind, in which its seed is upon the earth: and it was so.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
12 And the earth brought forth grass, herbs yielding seed after their kind, and trees yielding fruit, in which its seed is after their kind: and God saw that it was good.
Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
13 And it was evening and it was morning, the third day.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
14 And God said, Let there be lights in the expansion of the heaven to divide between the day and the night; and let them be for signs, and for seasons, and for days, and years;
Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
15 And let them be for lights in the expansion of the heaven, to give light upon the earth: and it was so.
zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
16 And God made the two great lights; the greater light to rule the day, and the lesser light to rule the night; and the stars.
Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
17 And God set them in the expansion of the heaven to give light upon the earth,
Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
18 And to rule by day and by night, and to divide between the light and the darkness: and God saw that it was good.
kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
19 And it was evening and it was morning, the fourth day.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
20 And God said, Let the waters bring forth abundantly moving creatures that have life, and fowl that may fly above the earth in the open expansion of the heaven.
Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
21 And God created the great sea-monsters, and every living creature that moveth, which the waters brought forth abundantly after their kind, and every winged fowl after its kind: and God saw that it was good.
Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
22 And God blessed them, saying, Be fruitful and multiply, and fill the waters in the seas, and let the fowl multiply on the earth.
Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
23 And it was evening and it was morning, the fifth day.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
24 And God said, Let the earth bring forth living creatures after their kind, cattle, and creeping things, and beasts of the earth after their kind: and it was so.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
25 And God made the beasts of the earth after their kind, and the cattle after their kind, and every thing that creepeth upon the earth after its kind: and God saw that it was good.
Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
26 And God said, Let us make man in our image, after our likeness; and they shall have dominion over the fish of the sea, and over the fowl of the heaven, and over the cattle, and over all the earth, and over every creeping thing that creepeth upon the earth.
Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
27 And God created man in his image, in the image of God created he him; male and female created he them.
Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
28 And God blessed them, and God said unto them, Be fruitful and multiply, and fill the earth, and subdue it; and have dominion over the fish of the sea, and over the fowl of the heaven, and over every living thing that moveth upon the earth.
Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
29 And God said, Behold I have given unto you every herb bearing seed, which is upon the face of all the earth, and every tree on which is the fruit of a tree yielding seed; to you it shall be for food.
Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
30 And to every beast of the earth, and to every fowl of the heaven, and to every thing that creepeth upon the earth, wherein there is life, [I have given] every green herb for food: and it was so.
Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
31 And God saw every thing that he had made, and behold, it was very good. And it was evening and it was morning, the sixth day.
Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

+ Genesis 1 >