< Genesis 44 >

1 And he commanded the superintendent of his house, saying, Fill the sacks of these men with food, as much as they can carry, and put every man's money in the mouth of his sack.
Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
2 And my cup, the silver cup, thou shalt put in the mouth of the sack of the youngest, and the money for his corn. And he did according to the word of Joseph which he had spoken.
Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
3 As soon as the morning was light, the men were sent away, they and their asses.
Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
4 They were gone out of the city, not yet far off, when Joseph said unto the superintendent of his house, Up, follow after the men; and when thou hast overtaken them, say unto them, Wherefore have ye returned evil for good?
Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
5 Is not this out of which my lord drinketh, and whereby indeed he divineth? ye have done evil in so doing.
Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
6 And he overtook them, and he spoke unto them these same words.
Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
7 And they said unto him, Wherefore will my lord speak such words as these? God forbid that thy servants should do any thing like this.
Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
8 Behold the money, which we found in the mouth of our sacks, we brought back unto thee out of the land of Canaan: how then should we steal out of thy lord's house silver or gold?
Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
9 With whomsoever of thy servants it be found, let him die; and we also will be bondmen unto thy lord.
Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
10 And he said, Now also let it be according to your words: he with whom it is found shall be my servant; but ye shall be blameless.
Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
11 And they made haste, and every one of them took down his sack to the ground, and every one opened his sack.
Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
12 And he searched, at the eldest he began, and at the youngest he left off; and the cup was found in Benjamin's sack.
Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
13 Then they rent their clothes, and every one loaded his ass, and they returned to the city.
Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
14 And Judah and his brothers came into Joseph's house, and he was yet there; and they fell down before him on the ground.
Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
15 And Joseph said unto them, What deed is this that ye have done? knew ye not that such a man as I can certainly divine?
Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
16 And Judah said, What shall we say unto my lord? what shall we speak? or how shall we justify ourselves? God hath found out the iniquity of thy servants: behold we are servants unto my lord, both we, as also he in whose hand the cup was found.
Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
17 And he said, God forbid that I should do this: the man in whose hand the cup was found, he shall be my servant; and as for you, go you up in peace unto your father.
Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
18 Then Judah came near unto him, and said, Pardon, my lord, let thy servant, I pray thee, speak a word in my lord's ears, and let not thy anger burn against thy servant; for thou art even as Pharaoh.
Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
19 My lord asked his servants, saying, Have ye a father, or a brother.
Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
20 And we said unto my lord, We have an old father, and a little child born in his old age; and his brother is dead, and he alone is left of his mother, and his father loveth him.
Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
21 And thou saidst unto thy servants, Bring him down unto me, that I may set my eye upon him.
“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
22 And we said unto my lord, The lad cannot leave his father; for if he should leave his father, he would die.
Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
23 And thou saidst unto thy servants, Except your youngest brother come down with you, ye shall not see my face any more.
Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
24 And it came to pass, when we came up unto thy servant my father, that we told him the words of my lord.
Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
25 And our father said, Go back and buy us a little food.
“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
26 And we said, We cannot go down: if our youngest brother be with us, then will we go down; for we cannot see the man's face, except our youngest brother be with us.
Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
27 And thy servant my father said unto us, Ye know that my wife bore me two sons;
“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
28 And the one went out from me, and I said, Surely he hath been torn to pieces; and I have not seen him up to this time.
Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
29 And if ye take this one also from me, and mischief befall him, ye will bring down my gray hairs with sorrow to the grave. (Sheol h7585)
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
30 And now, when I come to thy servant my father, and the lad be not with us; seeing that his life is bound up in the lad's life;
“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
31 It will come to pass, that when he seeth that the lad is not with us, he will die: and thy servants would thus bring down the gray hairs of thy servant our father with sorrow to the grave. (Sheol h7585)
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
32 For thy servant became surety for the lad unto my father, saying, If I bring him not unto thee, then shall I have sinned against my father all the days.
Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
33 Now therefore, I pray thee, let thy servant abide instead of the lad as bond-man to my lord; and let the lad go up with his brothers.
“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
34 For how shall I go up to my father, and the lad be not with me? I should perhaps be compelled to witness the evil which would come on my father.
Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

< Genesis 44 >