< Ezekiel 7 >
1 And the word of the Lord came unto me, saying,
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 And thou, son of man, thus hath said the Lord Eternal concerning the land of Israel, There is an end! the end is coming over the four corners of the land.
“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
3 Now cometh the end over thee, and I will let loose my anger against thee, and will judge thee according to thy ways, and I will lay upon thee all thy abominations.
Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4 And my eye shall not show pity upon thee, and I will not spare thee; for thy own ways will I lay upon thee, and thy abominations shall come in the midst of thee: and ye shall know that I am the Lord.
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5 Thus hath said the Lord Eternal, An evil, a peculiar evil, behold, is coming.
“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
6 An end is coming, there is coming the end: it waketh up against thee; behold, [the evil] cometh.
Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
7 The evil decree is come against thee, O thou inhabitant of the land: the time is come, near is the day of tumult, and not the joyful call on the mountains.
Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
8 Now will I in a short time pour out my fury over thee, and I will let out all my anger against thee, and I will judge thee according to thy ways, and I will lay upon thee all thy abominations.
Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
9 And my eye shall not show pity, and I will not spare: according to thy ways will I lay [evil] on thee, and thy abominations shall come in the midst of thee: and ye shall know that I am the Lord that smiteth.
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
10 Behold the day, behold, it is coming; the evil decree is gone forth; the staff hath blossomed, presumption hath budded;
“Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
11 The violence is grown up into the staff of wickedness: nothing is left of them, and nothing of their multitude, and nothing of theirs; and there shall be no lamenting for them.
Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
12 The time is coming, the day occurreth; let the buyer not rejoice, and let the seller not mourn; for wrath is against all her multitude.
Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13 For the seller shall not return to that which is sold, although their soul were yet alive; for the vision is against all her multitude; no one shall return; but the soul of every one is fastened to his iniquity, they do not strengthen themselves [to repent].
Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
14 They have blown the cornet, every one maketh himself ready; but no one goeth to the battle; for my wrath is against all her multitude.
“Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15 The sword is without, and the pestilence and the famine are within: he that is in the field shall die by the sword; and he that is in the city, him shall famine and pestilence devour.
Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
16 But they that escape of them shall escape, and they shall be on the mountains like the doves of the valleys, all of which are moaning, every one in his iniquity.
Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17 All hands become feeble, and all knees go into water.
Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18 And people gird themselves with sackcloth, and shuddering covereth them: and upon all faces there is shame, and upon all their heads there is baldness.
Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
19 Their silver shall they cast into the streets, and their gold shall be as though it were unclean: their silver and their gold shall not be able to deliver them on the day of the wrath of the Lord; they shall not satisfy their souls, and not fill their bowels; because it was the stumbling-block for their iniquity.
“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20 And as for the beauty of his ornament, which he had instituted for [their] pride: even therein did they make the images of their abominations, their detestable things; therefore have I rendered it unclean for them.
Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
21 And I will give it up into the hands of the strangers for a prey, and to the wicked of the earth for a spoil: and they shall pollute it.
Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
22 And I will turn away my face from them, and they shall pollute my place where I dwelt in secret; and therein shall barbarians enter and pollute it.
Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
23 Make chains; for the land is full of blood-guiltiness, and the city is full of violence.
“Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24 Therefore will I bring the worst of nations, and they shall take possession of their houses: I will also cause the pride of the mighty to cease; and their holy places shall be polluted.
Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25 Destruction cometh: and they will seek peace, but there shall be none.
Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26 Mishap shall come upon mishap, and report shall be spread upon report: and then will they seek a vision from the prophet; but the law shall be lost from the priest, and counsel from the ancients.
Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27 The king shall mourn, and the prince shall be clothed with distress, and the hands of the people of the land shall be powerless: after their way will I do unto them, and according to their own manners will I judge them; and they shall know that I am the Lord.
Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.