< Ezekiel 44 >

1 And he brought me back by the way of the outer gate of the sanctuary which looked toward the east: and it was locked.
Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
2 Then said the Lord unto me, This gate shall remain locked, it shall not be opened, and no man shall enter in by it; because the Lord, the God of Israel, hath entered in by it, therefore shall it remain locked.
Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
3 As for the prince, being the prince, he shall sit in it to eat bread before the Lord: by the way of the porch of that gate shall he enter, and by the way of the same shall he go out.
Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
4 Then brought he me by the way of the north gate before the house; and I looked, and, behold, the glory of the Lord filled the house of the Lord: and I fell upon my face.
Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
5 And the Lord said unto me, Son of man, direct thy mind, and see with thy eyes, and hear with thy ears all that I am speaking with thee concerning all the ordinances of the house of the Lord, and of all its laws; and direct thy mind to the entrance of the house, with every place of egress of the sanctuary.
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
6 And thou shalt say to the rebellious, to the house of Israel, Thus hath said the Lord Eternal, Ye have done enough with all your abominations, O house of Israel!
Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
7 In your having brought the sons of the stranger, uncircumcised in heart, and uncircumcised in flesh, to be in my sanctuary, to pollute it, even my house, while you were offering my food, the fat and the blood: so that they broke my covenant because of all your abominations.
Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
8 And [because] ye have not kept the charge of my holy things; but ye have set [those unworthy ones] as keepers of my charge in my sanctuary at your own pleasure.
Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
9 Thus hath said the Lord Eternal, No son of the stranger, uncircumcised in heart, or uncircumcised in flesh, shall enter into my sanctuary, of all the sons of the stranger that are in the midst of the children of Israel.
Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
10 But as respecteth the Levites that were gone away far from me, when Israel went astray, who went astray away from me, after their idols, they shall surely bear their iniquity;
“Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
11 And they shall be in my sanctuary, servants, appointed to watch at the gates of the house, and to be servants for the house: these are they that shall slay the burnt-offerings and the sacrifices for the people, and they shall stand before them to do the service for them.
Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
12 Because that they used to serve them before their idols, and have been unto the house of Israel as a stumbling-block of iniquity; therefore have I lifted up my hand against them, saith the Lord Eternal, and they shall bear their iniquity;
Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
13 And they shall not come near unto me, to officiate as priests unto me, nor to come near to any of my holy things, to the most holy things; but they shall bear their shame, yea, for their abominations which they have committed.
Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
14 And I will appoint them to be keepers of the charge of the house, for all the service thereof, and for all that shall be done therein.
Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
15 But the priests the Levites, the sons of Zadok, that kept the charge of my sanctuary when the children of Israel went astray from me, —these are they that shall come near unto me to minister unto me, and they shall stand before me to offer unto me the fat and the blood, saith the Lord Eternal:
“Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 These are they that shall enter into my sanctuary, and these shall come near to my table, to minister unto me; and they shall keep my charge.
Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
17 And it shall come to pass, that, when they enter in at the gates of the inner court, they shall clothe themselves with linen garments; and there shall no wool come upon them, when they minister in the gates of the inner court, and within the house.
“Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
18 Linen bonnets shall be upon their heads, and linen breeches shall be upon their loins: they shall not gird themselves with any thing that causeth sweat.
Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
19 And when they go forth into the outer court, into the outer court to the people: then shall they put off their garments wherein they have ministered, and they shall lay them down in the holy chambers; and they shall put on other garments, and they shall not mingle among the people with their garments.
Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
20 And their heads shall they not shave close, nor suffer their hair to grow long: they shall only crop [the hair of] their heads.
“‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
21 And wine shall none of the priests drink when they enter into the inner court.
Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
22 And a widow, or one that is divorced from her husband shall they not take to themselves as wives; but only virgins of the seed of the house of Israel; but whatever widow it may be, the [common] priests may take.
Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
23 And my people shall they teach the difference between the holy and profane, and that between the unclean and the clean shall they make known unto them.
Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
24 And in a controversy shall they stand up to judge, according to my ordinances shall they decide it: and my laws and my statutes at all my festivals shall they observe, and my sabbaths shall they sanctify.
“‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
25 And to a dead person shall they not come to defile themselves; but on father, or on mother, or on son, or on daughter, on brother, or on sister that hath had no husband, may they defile themselves.
“‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
26 And after he is become clean, —they shall reckon unto him seven days, —
Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
27 Then shall he on the day that he cometh into the sanctuary, into the inner court, to minister in the sanctuary, offer his sin-offering, saith the Lord Eternal.
Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
28 And it shall be unto them as an inheritance, I am their inheritance: and any possession shall you not give them in Israel, I am their possession.
“‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
29 The meat-offering, and the sin-offering, and the trespass-offering—these shall they eat; and every devoted thing in Israel shall belong to them.
Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
30 And the first of all kinds of first-fruits of all, and every kind of heave-offering of every thing of all your heave-offerings, shall belong to the priests; and the first of your dough shall you give to the priest, to cause a blessing to rest on thy house.
Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
31 Any thing that hath died of itself, or that is torn, whether it be fowl or beast, shall the priests not eat.
Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”

< Ezekiel 44 >