< Ezekiel 39 >

1 But thou, O son of man, prophesy against Gog, and say, Thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will be against thee O Gog, the prince of Rosh, Meshech and Thubal;
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 And I will derange thee, and lead thee astray, and will cause thee to come up from the farthest ends of the north; and I will bring thee upon the mountains of Israel;
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 And I will strike thy bow out of thy left hand, and thy arrows will I cause to fall out of thy right hand.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Upon the mountains of Israel shalt thou fall, thou, and all thy armies, and the people that are with thee: unto the ravenous birds, to every thing that hath wings, and to the beasts of the field, do I give thee for food.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Upon the open field shalt thou fall; for I have spoken it, saith the Lord Eternal.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 And I will send a fire against Magog, and against those that dwell in the isles in safety: and they shall know that I am the Lord.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 And my holy name will I make known in the midst of my people Israel; and I will not permit my holy name to be profaned any more: and the nations shall know that I am the Lord, Holy in Israel.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Behold, it cometh, and it taketh place, saith the Lord Eternal; this is the day whereof I have spoken.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 And the inhabitants of the cities of Israel shall go forth, and shall burn and make fire for heating of the weapons, and shields and bucklers, of bows and of arrows, and of hand-staves, and of spears; and they shall feed with them the fire for seven years;
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 And they shall take no wood out of the field, nor cut down any out of the forests; for with weapons shall they feed the fire: and they shall spoil those that spoiled them, and plunder those that plundered them, saith the Lord Eternal.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 And it shall come to pass on that day, that I will give unto Gog a place there for a grave in Israel, the valley where people pass over to the east of the sea; and it shall stop the passengers [from passing]: and they shall bury there Gog and all his multitude, and they shall call it The valley of the multitude of Gog.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 And the house of Israel shall be burying them, in order to cleanse the land, during seven months.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Yea, all the people of the land shall bury them; and it shall be to them as a renown on the day that I glorify myself, saith the Lord Eternal.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 And men constantly devoted to this shall they set apart to pass through the land, to bury with those that pass through those that remain upon the face of the earth, to cleanse it; at the end of seven months shall they make a search.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 And those that thus travel will pass through the land; and when any one seeth a human bone, then will he set up a sign by it, till the buriers have buried it in the valley of the multitude of Gog.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 And also the name of the city shall be Hamonah. Thus shall they cleanse the land.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 And thou, O son of man, thus hath said the Lord Eternal, Say unto the birds, to every thing that hath wings, and to every beast of the field, Assemble yourselves, and come; gather yourselves from every side to my sacrifice that I do slaughter for you, as a great sacrifice upon the mountains of Israel, that ye may eat flesh, and drink blood.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 The flesh of the mighty shall ye eat, and the blood of the princes of the earth shall ye drink, —wethers, lambs, and he-goats, bullocks, fatlings of Bashan are they all of them.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 And ye shall eat fat till ye be sated, and ye shall drink blood till ye be drunken, from my sacrifice which I have slaughtered for you.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 And ye shall be sated at my table on horses and chariot-teams, on mighty men, and on all men of war, saith the Lord Eternal.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 And I will display my glory among the nations: and all the nations shall see my punishment that I execute, and my hand that I lay on them.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 And the house of Israel shall acknowledge that I am the Lord their God from that day and forward.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 And the nations shall know that for their iniquity did the house of Israel go into exile; because they had trespassed against me, and I had hidden my face from them; and I gave them up therefore into the hand of their oppressors, and they all fell by the sword.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 According to their uncleanness, and according to their transgressions did I deal with them, and hid my face from them.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Therefore thus hath said the Lord Eternal, Now will I bring back again the captivity of Jacob, and I will have mercy upon the whole house of Israel, and will be zealous for my holy name;
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 And they shall feel their disgrace, and all their trespass whereby they had trespassed against me, when they dwelt in their land in safety, with none to make them afraid:
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 When I bring them back again from the people, and gather them out of the land of their enemies, and sanctify myself on them before the eyes of the many nations.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 And they shall know that I am the Lord their God; because I had exiled them among the nations, but gather them now unto their own land, and leave none of them any more there.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 And I will not hide my face any more from them; for I will have poured out my spirit over the house of Israel, saith the Lord Eternal.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 39 >