< Ezekiel 37 >

1 There came over me the inspiration of the Lord, and he carried me out in the spirit of the Lord, and set me down in the midst of the valley which was full of bones;
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 And he caused me to pass by them all round about; and, behold, there were very many of them on the surface of the valley; and, lo, they were very dry.
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 And he said unto me, Son of man, can these bones live! And I said, O Lord Eternal, thou alone knowest this.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 And he said unto me, Prophesy over these bones, and say unto them, O ye dry bones, hear ye the word of the Lord.
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 Thus hath said the Lord Eternal unto these bones, Behold, I will bring a spirit into you, and ye shall live;
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 And I will lay sinews upon you, and bring up flesh upon you, and draw over you a skin, and put a spirit in you, and ye shall live: and ye shall experience that I am the Lord.
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 And so I prophesied as I had been commanded: and there was a sound, as I prophesied, and behold there was a rustling noise, and the bones came together, bone to its bone.
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 And I looked, and behold, there were sinews upon them, and the flesh came up, and the skin was drawn over them above; but no spirit was in them.
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 Then said he unto me, Prophesy unto the spirit; prophesy, son of man, and say to the spirit, Thus hath said the Lord Eternal, From the four winds come, O spirit, and breathe into these slain ones, that they may live.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 And I prophesied as he had commanded me, and there came into them the spirit, and they lived, and stood up upon their feet, an exceedingly great army.
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 Then said he unto me, Son of man, these bones are the whole house of Israel: behold, they say, Dried are our bones, and lost is our hope; we are quite cut off.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 Therefore prophesy and say unto them, Thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will open your graves, and I will cause you to come up out of your graves, O my people, and I will bring you into the land of Israel.
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 And ye shall know that I am the Lord, when I open your graves, and when I cause you to come up out of your graves, O my people.
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 And I will put my spirit in you, and ye shall live, and I will place you in your own land: and ye shall acknowledge that I the Lord have spoken it, and done it, saith the Lord.
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 And the word of the Lord came unto me, saying,
Yehova anandiyankhula kuti:
16 But thou, son of man, take unto thyself one stick of wood, and write upon it, “For Judah, and for the children of Israel his companions;” then take another stick, and write upon it, “For Joseph, —the stick of Ephraim, and for all the house of Israel his companions:”
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 And join them one to the other unto thee as one stick; and they shall become one in thy hand.
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 And if the children of thy people should say unto thee, saying, Wilt thou not tell us what thou meanest by these?
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 [Then] speak unto them, Thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will take the stick of Joseph, —which is in the hand of Ephraim, —and the tribes of Israel his companions, and will lay them upon him, even the stick of Judah, and make them into one stick, and they shall be one in my hand.
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 And the sticks whereon thou shalt have written shall be in thy hand before their eyes.
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 And speak unto them, Thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will take the children of Israel from among the nations, whither they are gone, and I will gather them from every side, and bring them unto their own land;
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 And I will make them into one nation in the land, on the mountains of Israel; and one king shall be to them all for king; and they shall not be any more two nations, nor shall they at any time be divided into two kingdoms any more:
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 Neither shall they defile themselves any more with their idols, and with their detestable things, and with all their transgressions; but I will save them out of all their dwelling-places, wherein they have sinned, and I will cleanse them, and they shall be unto me for a people, and I will be to them for a God.
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 And my servant David shall be king over them; and one shepherd shall be for them all: and in my ordinances shall they walk, and my statutes shall they observe, and do them.
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 And they shall dwell in the land that I have given unto my servant, unto Jacob, wherein your fathers have dwelt; and they shall dwell therein, they, and their children, and their children's children for ever: and David my servant shall be prince unto them for ever.
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 And I will make with them a covenant of peace, an everlasting covenant shall it be with them: and I will multiply them, and I will set my sanctuary in the midst of them for evermore.
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 My dwelling also shall be with them, and I will be unto them for a God; and they shall be unto me as a people.
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 And the nations shall know that I am the Lord who sanctify Israel, when my sanctuary will be in the midst of them for evermore.
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”

< Ezekiel 37 >