< Ezekiel 32 >

1 And it came to pass in the twelfth year, in the twelfth month, on the first day of the month, that the word of the Lord came unto me, saying,
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Son of man, take up a lamentation for Pharaoh the king of Egypt, and say unto him, Thou didst deem thyself like a young lion among the nations: while thou art as a crocodile in the seas; and thou issuedst forth with thy rivers, and madest turbid the waters with thy feet, and didst stir up their rivers.
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
3 Thus hath said the Lord Eternal, I will therefore spread out my net over thee through the assemblage of many people, and they shall draw thee up in my net.
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
4 Then will I cast thee upon the land, upon the open field will I hurl thee, and will cause all the fowls of the heaven to dwell upon thee, and I will satisfy off thee the beasts of all the earth.
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
5 And I will lay thy flesh upon the mountains, and fill the valleys with thy carcass.
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
6 I will also saturate the land wherein thou swimmest with thy blood, even to the mountains; and the ravines shall be full of thee.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
7 And I will cover up the heavens, when thou art quenched, and make their stars obscure: the sun will I cover up with a cloud, and the moon shall not let shine her light.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
8 All the light-dispensing lights of the heavens—these will I make obscure because of thee, and I will lay darkness upon thy land, saith the Lord Eternal.
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
9 And I will aggrieve the heart of many people, when I bring those who are broken off from thee among the nations, into countries which thou hast not known.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Yea, I will make many people amazed at thee, and on their kings the hair shall stand on end because of thee, when I brandish my sword before their faces: and they shall tremble at every moment, every man for his own life, on the day of thy downfall.
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
11 For thus hath said the Lord Eternal, The sword of the king of Babylon shall come over thee.
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 By the swords of the mighty will I cause thy multitude to fall, the fiercest of nations are all of them: and they shall destroy the pride of Egypt, and all her multitude shall be annihilated.
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 And I will cause to vanish all her beasts from beside the great waters; and the foot of man shall not make them turbid any more, nor shall the hoofs of beasts make them turbid.
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Then will I make clear their waters, and cause their rivers to flow like oil, saith the Lord Eternal;
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
15 When I render the land of Egypt desolate and wasted, the country bereft of what now filleth it, when I smite all those that dwell therein: and they shall know that I am the Lord.
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
16 This is the lamentation wherewith they shall lament for her; the daughters of the nations shall lament for her: for Egypt, and for all her multitude, shall they lament with it, saith the Lord Eternal.
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
17 And it came to pass in the twelfth year, on the fifteenth day of the month, that the word of the Lord came unto me, saying,
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
18 Son of man, moan for the multitude of Egypt, and say that it shall go down, yea, she, and the daughters of powerful nations, unto the land of the nether world, with those that go down to the pit.
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
19 Whom dost thou surpass in loveliness? go down [then], and be thou laid with the [other] uncircumcised.
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
20 In the midst of those that are slain by the sword shall they fall: to the sword is she given up; drag her away and all her multitudes.
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
21 Then will speak of him the strongest among the mighty out of the midst of the nether world with those that once helped him, They are gone down, there lie the uncircumcised, —slain by the sword. (Sheol h7585)
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
22 There is Asshur and all his assemblage; round about him are his graves; all of them the slain that are fallen by the sword;
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
23 Whose graves are placed in the lowest depth of the pit, and his assemblage is round about his grave; all of them are slain, fallen by the sword, who once spread terror in the land of the living.
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
24 There is 'Elam and all her multitude round about her grave, all of them the slain, that are fallen by the sword, who are gone down uncircumcised into the land of the nether world, who once spread their terror in the land of the living; and they have borne their confusion with those that go down to the pit.
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
25 In the midst of the slain have they set a couch for her with all her multitude; all round about are her graves; all of them are uncircumcised, slain by the sword; because their terror was once spread in the land of the living; and they have borne their confusion with those that go down to the pit: in the midst of the slain was she placed.
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
26 There is Meshech, Thubal, and all her multitude; all round about her are her graves: all of them are the uncircumcised, slain by the sword; because they once spread their terror in the land of the living.
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
27 And those who are fallen of the uncircumcised shall not lie with the mighty, who are gone down to the nether world with their weapons of war, while men laid their swords under their heads, and the [instruments of] their iniquities were upon their bones; for the terror of the mighty was in the land of the living. (Sheol h7585)
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
28 But thou shalt be broken in the midst of the uncircumcised, and shalt lie with those that are slain by the sword.
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
29 There are Edom, her kings, and all her princes, who are laid despite their prowess by those that are slain by the sword: they shall lie with the uncircumcised, and with those that go down to the pit.
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
30 There are the chieftains of the north, all of them, and all the Zidonians, who are gone down with the slain: despite the terror they excited through their prowess are they made ashamed; and they lie uncircumcised with those that are slain by the sword, and bear their confusion with those that go down to the pit.
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
31 These shall Pharaoh see, and he shall be comforted over all his multitude: slain by the sword are Pharaoh and all his army, saith the Lord Eternal.
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
32 For I spread my terror in the land of the living; and he shall be laid in the midst of the uncircumcised with those that are slain by the sword, —yea, Pharaoh and all his multitude, saith the Lord Eternal.
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 32 >