< Ezekiel 29 >

1 In the tenth year, in the tenth month, on the twelfth day of the month, came the word of the Lord unto me, saying,
Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Son of man, set thy face against Pharaoh the king of Egypt, and prophesy against him, and against all Egypt.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
3 Speak and say, Thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will be against thee, O Pharaoh king of Egypt, the great crocodile that lieth in the midst of his streams, who hath said, Mine is my stream, and I have made it for myself.
Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
4 But I will put hooks in thy jaws, and I will fasten the fish of thy streams on thy scales; and I will bring thee up out of the midst of thy streams, with all the fish of thy streams which shall stick fast on thy scales.
Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
5 And I will cast thee out into the wilderness, thee with all the fish of thy streams; upon the open field shalt thou fall; thou shalt not be brought in, nor gathered up: to the beasts of the field and to the fowls of the heaven have I given thee for food.
Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
6 And all the inhabitants of Egypt shall know that I am the Lord; because they have been a reed-staff to the house of Israel.
Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
7 When they took hold of thee with the hand, thou wast cracked, and didst rend for them all the shoulder: and when they leaned upon thee, thou wast broken, and madest all their loins to be at a stand.
Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
8 Therefore thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will bring a sword upon thee, and I will cut off out of thee man and beast.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
9 And the land of Egypt shall be changed into a waste and ruin, and they shall know that I am the Lord; because he hath said, The stream is mine, and I have made it.
Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
10 Therefore, behold, I will be against thee, and against thy streams, and I will render the land of Egypt a mass of ruins, a waste, and a wilderness, from Migdol to Seveneh even up to the border of Ethiopia.
nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
11 There shall not pass through it the foot of man, and the foot of beast shall not pass through it, and it shall not be inhabited forty years.
Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
12 And I will render the land of Egypt a desolate land in the midst of desolated countries, and her cities among the cities that are ruined shall be desolate forty years: and I will scatter the Egyptians among the nations, and will disperse them through the countries.
Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
13 For thus hath said the Lord Eternal, [only] at the end of forty years will I gather the Egyptians from the people whither they shall have been scattered;
“‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
14 And I will bring back the captivity of Egypt, and will cause them to return into the land of Pathros, into the land of their own origin: and they shall be there an unimportant kingdom.
Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
15 Among the kingdoms it shall be the lowest; neither shall it raise itself any more above the nations: and I will diminish them, that they shall no more rule over the nations.
Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
16 And it shall be no more unto the house of Israel for a dependence, bringing [their] iniquity to remembrance, when they turned after them: and they shall know that I am the Lord Eternal.
Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
17 And it came to pass in the seven and twentieth year, in the first month, on the first of the month, that the word of the Lord came unto me, saying,
Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
18 Son of man, Nebuchadrezzar the king of Babylon hath caused his army to perform a great service against Tyre; every head hath been made bald, and every shoulder hath been rubbed sore: yet no reward hath come to him or to his army from Tyre, for the service that he hath performed against it.
“Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
19 Therefore thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will give unto Nebuchadrezzar the king of Babylon the land of Egypt; and he shall carry away its multitude, and take its spoil, and plunder its prey: and this shall be the reward for his army.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
20 As his recompense for that which he hath served against it, have I given him the land of Egypt, for that which they had done against me, saith the Lord Eternal.
Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
21 On that day will I cause to grow a horn for the house of Israel, and unto thee will I open the mouth in the midst of them: and they shall know that I am the Lord.
“Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 29 >