< Ezekiel 2 >

1 And he said unto me, Son of man, stand up upon thy feet, and I will speak with thee.
Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
2 And a spirit entered into me as he spoke unto me, and it placed me upon my feet, and I heard him that spoke unto me.
Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
3 And he said unto me, Son of man, I send thee to the children of Israel, to rebellious tribes that have rebelled against me: they and their fathers have transgressed against me, even until this very day.
Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
4 And the children are impudent of face, and obdurate of heart: I send thee unto them; and thou shalt say unto them, Thus hath said the Lord Eternal.
Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
5 And they, whether they will hear, or whether they will forbear, [for they are a rebellious family, ] shall yet know that a prophet hath been among them.
Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
6 And thou, son of man, —thou shalt not be afraid of them, and of their words thou shalt have no fear, though they be briers and thorns with thee, and thou dost dwell among scorpions: of their words be not afraid, and at their presence be not dismayed; for they are a rebellious family.
Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
7 And thou shalt speak my words unto them, whether they will hear, or whether they will forbear; for they are rebellious.
Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
8 But thou, son of man, hear what I am speaking unto thee, Be not thou rebellious like this rebellious family: open thy mouth, and eat what I give unto thee.
Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
9 And then I looked, and behold, a hand was stretched out toward me; and, lo, a roll-book was therein;
Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
10 And he spread it out before me; and it was written within and without: and there were written therein lamentations, and dirges, and woe.
Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.

< Ezekiel 2 >