< Exodus 22 >

1 If a man steal an ox or a sheep, and kill it, or sell it: five oxen shall he restore for one ox, and four sheep for one sheep.
“Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
2 If a thief be found while breaking in, and be smitten so that he die, there shall no blood be shed for him.
“Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
3 If the sun be risen upon him, there shall be blood shed for him; he shall make full restitution; if he have nothing, then shall he be sold for his theft.
Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
4 If the thing stolen be actually found in his hand alive, whether it be ox, or ass, or sheep, he shall restore double.
“Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
5 If a man cause a field or vineyard to be eaten off, and he let his beasts enter, and they feed in another man's field; with the best of his own field, and with best of his own vineyard, shall he make restitution.
“Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
6 If a fire break out, and meet with thorns, so that stacks of corn, or the standing corn, or the field, be consumed thereby, he that kindled the fire shall surely make restitution.
“Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
7 If a man do deliver unto his neighbor money or vessels to keep, and it be stolen out of the man's house: if the thief be found, he shall pay double.
“Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
8 If the thief be not found, then shall the master of the house be brought unto the judges, [to swear] that he have not stretched out his hand against his neighbor's goods.
Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
9 For all manner of trespass, for ox, for ass, for lamb, for raiment, or for any manner of lost thing, of which he can say, This is it, before the judges shall come the cause of both parties, and he, whom the judges may condemn, shall pay double unto his neighbor.
Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
10 If a man deliver unto his neighbor an ass, or an ox, or a lamb, or any beast, to keep; and it die, or be hurt, or driven away, no man seeing it:
“Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
11 Then shall an oath of the Lord be between them both, that he have not stretched out his hand against his neighbor's goods; and the owner of it shall accept this, and he shall not make it good.
ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
12 But if it be stolen from him, he shall make restitution unto the owner thereof.
Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
13 If it be torn in pieces, then let him bring it as evidence; that which was torn he shall not make good.
Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
14 And if a man borrow aught of his neighbor, and it be hurt, or die, the owner thereof not being with it, he shall surely make it good.
“Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
15 But if the owner thereof be with it, he shall not make it good; if it be a hired thing, the loss is included in its hire.
Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
16 And if a man seduce a virgin that is not betrothed, and lie with her, he shall surely endow her to be his wife.
“Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
17 If her father refuse to give her unto him, he shall pay money according to the dowry of virgins.
Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
18 Thou shalt not suffer a witch to live.
“Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
19 Whosoever lieth with a beast shall surely be put to death.
“Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
20 He that sacrificeth unto any god, save unto the Lord only, shall be utterly destroyed.
“Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
21 And a stranger thou shalt not vex, and shalt not oppress him; for strangers ye were in the land of Egypt.
“Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
22 Ye shall not afflict any widow, or fatherless child.
“Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
23 If thou afflict him in any wise; [for if he cry at all unto me, I will surely hear his cry: ]
Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
24 My wrath shall wax hot, and I will slay you with the sword; and your wives shall be widows, and your children fatherless.
Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
25 If thou lend money to my people, to the poor by thee, thou shalt not be to him as a lender of money; thou shalt not lay upon him usury.
“Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
26 If thou take at all thy neighbor's raiment in pledge, thou shalt restore it unto him by the time the sun goeth down;
Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
27 For it is his only covering, it is his raiment for his skin; wherein shall he sleep? and it shall come to pass, when he crieth unto me, that I will hear; for I am gracious.
chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
28 The judges thou shalt not revile; and a ruler among thy people thou shalt not curse.
“Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
29 The first of thy ripe fruits, and of thy liquors, shalt thou not delay to offer; the first-born of thy sons shalt thou give unto me.
“Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
30 In like manner shalt thou do with thy ox, with thy sheep; seven days it shall be with its dam; on the eighth day thou shalt give it me.
Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
31 And holy men shall ye be unto me: and flesh that is torn of beasts in the field, shall ye not eat; to the dogs shall ye cast it.
“Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”

< Exodus 22 >