< Exodus 2 >

1 And there went a man of the house of Levi, and took a daughter of Levi.
Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
2 And the woman conceived, and bore a son; and when she saw him that he was a goodly child, she hid him three months.
Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
3 And when she could no longer hide him, she took for him a box of bulrushes, and daubed it with slime and with pitch; and she put the child therein, and laid it amidst the flags by the brink of the river.
Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
4 And his sister placed herself afar off, to ascertain what would be done to him.
Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
5 And the daughter of Pharaoh came down to wash herself at the river; and her maidens walked along by the side of the river; and when she saw the box among the flags, she sent her maid and fetched it.
Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
6 And she opened it, and saw the child, and, behold, it was a weeping boy; and she had compassion on him, and said, This is one of the Hebrews' children.
Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
7 Then said his sister to Pharaoh's daughter, Shall I go and call thee a nurse of the Hebrew women, that she may nurse for thee the child?
Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
8 And Pharaoh's daughter said to her, Go; and the maiden went and called the mother of the child.
Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
9 And Pharaoh's daughter said unto her, Take away this child, and nurse him for me, and I will give thee thy wages; and the woman took the child, and nursed him.
Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
10 And the child grew up, and she brought him unto Pharaoh's daughter, and he became to her as a son; and she called his name Moses; and she said, Because out of the water have I drawn him.
Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
11 And it came to pass in those days, when Moses was grown up, that he went out unto his brethren, and looked on their burdensome labors; and he saw an Egyptian man smiting a Hebrew man, one of his brethren.
Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
12 And he looked this way and that way, and when he saw that there was no one by, he smote the Egyptian, and hid him in the sand.
Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
13 And when he went out the second day, behold, two Hebrew men were striving together; and he said unto him that was in the wrong, Wherefore smitest thou thy fellow?
Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
14 And he said, Who made thee a chief and a judge over us? intendest thou to kill me, as thou hast killed the Egyptian! And Moses feared, and said, Surely the thing is become known.
Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
15 And Pharaoh heard this thing, and he sought to slay Moses; but Moses fled from the face of Pharaoh, and tarried in the land of Midian, and he sat down by a well.
Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
16 Now the priest of Midian had seven daughters; and they came and drew water, and filled the troughs to water their father's flock.
Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
17 And the shepherds came and drove them away; but Moses arose and helped them, and watered their flock.
Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
18 And when they came to Reuel their father, he said, Wherefore are ye come home so soon today?
Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
19 And they said, An Egyptian man delivered us out of the hand of the shepherds; and he also drew water for us, and watered the flock.
Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
20 And he said unto his daughters, And where is he? wherefore have ye left the man? call him, that he may eat bread.
Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
21 And Moses was content to dwell with the man; and he gave Zipporah his daughter to Moses.
Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
22 And she bore a son, and he called his name Gershom; for he said, I have been a stranger in a foreign land.
Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
23 And it came to pass in this long time, that the king of Egypt died; and the children of Israel sighed by reason of the bondage, and they cried; and their complaint came up unto God by reason of the bondage.
Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
24 And God heard their groaning, and God remembered his covenant with Abraham, with Isaac, and with Jacob.
Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
25 And God looked upon the children of Israel, and God took cognizance of them.
Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

< Exodus 2 >