< Esther 6 >
1 In that night sleep fled from the king, and he ordered to bring in the book of the memorable events of the chronicles; and they were read before the king.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 And it was found written, that Mordecai had told of Bigthana and Theresh, two chamberlains of the king, of those who kept the door, who had sought to lay [their] hand on king Achashverosh.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 And the king said, What honor and distinction have been done to Mordecai for this? Then said the king's young men, his servants, There hath nothing been done with him.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 And the king said, Who is in the court? Now Haman was come into the outer court of the king's house, to say unto the king to hang Mordecai on the gallows which he had prepared for him.
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 And the king's young men said unto him, Behold, Haman is standing in the court. And the king said, Let him come in.
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 So Haman came in; and the king said unto him, What shall be done with the man whom the king desireth to honor? And Haman said in his heart, To whom would the king desire to do honor more than to myself?
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 Haman therefore said to the king, [For] the man whom the king desireth to honor,
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 Let them bring a royal apparel which the king hath worn, and a horse on which the king hath ridden, and let there be placed a royal crown on his head.
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 And let the apparel and the horse be given into the hand of one of the king's princes, of the most noble, that they may array the man whom the king desireth to honor, and let them cause him to ride on the horse through the streets of the city, and proclaim before him, Thus shall be done to the man whom the king desireth to honor.
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 Then said the king to Haman, Make haste, take the apparel and the horse, as thou hast spoken, and do thus to Mordecai the Jew, that sitteth at the king's gate: leave out nothing of all that thou hast spoken.
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 And Haman then took the apparel and the horse, and arrayed Mordecai, and caused him to ride through the streets of the city, and proclaimed before him, Thus shall be done unto the man whom the king desireth to honor.
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 And Mordecai thereupon returned to the king's gate; but Haman hastened to his house, mourning, and having his head covered.
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 And Haman related to Zeresh his wife and to all his friends all that had befallen him: then said unto him his wise men and Zeresh his wife, If Mordecai, before whom thou hast begun to fall, be of the seed of the Jews, thou wilt not prevail against him, but thou wilt surely fall before him.
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 They were yet speaking with him, when the king's chamberlains arrived, and they hastened to bring Haman unto the banquet which Esther had prepared.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.