< Deuteronomy 11 >

1 Thou shalt therefore love the Lord thy God, and keep his charge, and his statutes, and his ordinances, and his commandments, all the days.
Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
2 And ye shall know this day, that [I speak] not with your children who have not known, and who have not seen the chastisement of the Lord your God, his greatness, his strong hand, and his outstretched arm;
Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
3 And his signs, and his acts, which he displayed in the midst of Egypt, unto Pharaoh the king of Egypt, and unto all his land;
zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
4 And what he did unto the army of Egypt, unto its horses, and to its chariots; over whom he caused the water of the Red Sea to flow, as they pursued after you, and whom the Lord destroyed unto this day;
zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
5 And what he did unto you in the wilderness, until ye came unto this place;
Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
6 And what he did unto Dathan and Abiram, the sons of Eliab, the son of Reuben; how the earth opened her mouth, and swallowed them up, and their households, and their tents, and all the living substance that followed them, in the midst of all Israel;
ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
7 But it is your own eyes which have seen all the great acts of the Lord which he hath done.
Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
8 Ye shall therefore keep all the commandment which I command you this day, that ye may be strong, and go in and take possession of the land, whither ye go over to possess it;
Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
9 And in order that ye may live many days in the land, which the Lord hath sworn unto your fathers to give unto them and to their seed, a land flowing with milk and honey.
ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
10 For the land, whither thou goest in to possess it, is not like the land of Egypt, from where ye came out, where thou sowest thy seed, and waterest it with thy foot, as a garden of herbs;
Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
11 But the land, whither ye go over to possess it, is a land of mountains and valleys, from the rain of heaven doth it drink water.
Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
12 A land which the Lord thy God careth for; always are the eyes of the Lord thy God upon it, from the beginning of the year even unto the end of the year.
Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
13 And it shall come to pass, if ye will hearken diligently unto my commandments which I command you this day, to love the Lord your God, and to serve him with all your heart and with all your soul,
Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
14 That I will send rain for your land in its due season, the first rain and the latter rain, that thou mayest gather in thy corn, and thy wine, and thy oil.
pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
15 And I will give grass in thy field for thy cattle; and thou shalt eat and be satisfied,
Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
16 Take heed to yourselves, that your heart be not deceived, and ye turn aside, and serve other gods, and worship them;
Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
17 [For] then the Lord's wrath will be kindled against you, and he will shut up the heavens that there be no rain, and the land will not yield her products; and ye shall perish quickly from off the good land which the Lord giveth unto you.
Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
18 Therefore shall ye lay up these my words in your heart and in your soul; and ye shall bind them for a sign upon your hand, and they shall be as frontlets between your eyes.
Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
19 And ye shall teach them to your children, to speak of them when thou sittest in thy house, and when thou walkest by the way, and when thou liest down, and when thou risest up.
Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
20 And thou shalt write them upon the door-posts of thy house, and upon thy gates.
Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
21 In order that your days may be multiplied, and the days of your children, in the land which the Lord swore unto your fathers to give unto them, as the days of the heavens over the earth.
kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
22 For if ye will diligently keep all this commandment which I command you, in order to do it, to love the Lord your God, to walk in all his ways, and to cleave unto him:
Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
23 Then will the Lord drive out all these nations from before you, and ye shall supplant nations greater and mightier than yourselves.
Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
24 Every place whereon the sole of your foot may tread shall be yours: from the wilderness and the Lebanon, from the river, the river Euphrates, even unto the Western Sea shall be your boundary.
Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
25 There shall no man be able to stand up before you; the dread of you and the fear of you will the Lord your God lay upon all the land which ye may tread upon, as he hath spoken unto you.
Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
26 Behold, I lay before you this day a blessing and a curse:
Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
27 The blessing, if ye will hearken unto the commandments of the Lord your God, which I command you this day;
dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
28 And the curse, if ye will not hearken unto the commandments of the Lord your God, and ye turn aside out of the way which I command you this day, to go after other gods, which ye know not.
Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
29 And it shall come to pass, when the Lord thy God shall have brought thee in unto the land whither thou goest to possess it, that thou shalt put the blessing upon mount Gerizzim, and the curse upon mount 'Ebal.
Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
30 Behold, they are on the other side of the Jordan, far away in the direction of the going down of the sun, in the land of the Canaanites, who dwell in the plain, opposite Gilgal, near the grove of Moreh.
Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
31 For ye are about to pass over the Jordan to go in to take possession of the land which the Lord your God giveth you; and ye will possess it, and dwell therein.
Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
32 And ye shall then observe to do all the statutes and ordinances which I set before you this day.
mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.

< Deuteronomy 11 >