< 2 Samuel 15 >
1 And it came to pass after this, that Abshalom provided for himself a chariot and horses, and fifty men who ran before him.
Patapita nthawi, Abisalomu anadzipezera galeta ndi akavalo pamodzi ndi amuna makumi asanu amene amathamanga patsogolo pake.
2 And Abshalom rose up early, and stood on the side of the way to the gate: and it happened, that whenever a man who had a controversy came to the king for judgment, Abshalom called to him, and said, From what city art thou? And he said, Thy servant is from one of the tribes of Israel.
Iye amadzuka mmamawa ndi kuyima pa njira yopita ku chipata cha mzinda. Munthu wina aliyense akakhala ndi zodandaula zopita nazo kwa mfumu kuti akaweruze, Abisalomu amamuyitana iye ndi kumufunsa kuti, “Kodi ukuchokera ku limodzi mwa mafuko a Israeli?”
3 And Abshalom said unto him, See, thy words are good and right; but no one listeneth to thee on the part of the king.
Kenaka Abisalomu amanena kwa iye kuti, “Taona, madandawulo ako ndi abwino ndi oyenera, koma palibe woyimira mfumu woti akumvere.”
4 And Abshalom said, Oh, if there were but one to appoint me judge in the land, so that every man who may have any controversy or cause might come unto me, and I would do him justice!
Ndipo Abisalomu amawonjezera kunena kuti, “Ine ndikanangosankhidwa kukhala woweruza mʼdziko muno bwenzi munthu aliyense amene ali ndi madandawulo kapena milandu akubwera kwa ine ndipo ndikanaonetsetsa kuti chilungamo chachitika.”
5 And it happened, that when a man came nigh to bow down to him, he used to put forth his hand, and laid hold of him, and kissed him.
Ndipo nthawi zonse amati munthu akasendera pafupi ndi kumugwandira, Abisalomu amatambalitsa dzanja lake, kumuyimiritsa munthuyo ndi kupsompsona.
6 And Abshalom did after this manner to all Israel that came to the king for judgment: and thus did Abshalom steal the heart of the men of Israel.
Abisalomu amachitira izi Aisraeli onse amene amabwera kwa mfumu kuti adzaweruzidwe ndipo Abisalomuyo anagwira mtima anthu a mu Israeli.
7 And it came to pass at the end of forty years, that Abshalom said unto the king, Let me go, I pray thee, and fulfill my vow, which I have vowed unto the Lord, at Hebron.
Patapita zaka zinayi Abisalomu anati kwa mfumu, “Loleni ndipite ku Hebroni kuti ndikakwaniritse lonjezo limene ndinachita kwa Yehova.
8 For thy servant vowed a vow while I abode at Geshur in Syria, saying, If the Lord will ever bring me back again to Jerusalem, then will I serve the Lord.
Pamene mtumiki wanu amakhala ku Gesuri ku Aramu, anachita lonjezo ili: ‘Ngati Yehova adzandibweretsadi ku Yerusalemu, ndidzapembedza Yehovayo mu Hebroni.’”
9 And the king said unto him, Go in peace: and he arose, and went to Hebron.
Mfumu inati kwa iye, “Pita mu mtendere” Kotero iye anapita ku Hebroni.
10 But Abshalom sent spies throughout all the tribes of Israel, saying, When ye hear the sound of the cornet, then shall ye say, Abshalom is become king at Hebron.
Ndipo Abisalomu anatuma amithenga ake mwamseri kwa mafuko onse a Israeli kukanena kuti, “Mukangomva kulira kwa malipenga pamenepo munene kuti, ‘Abisalomu ndiye mfumu mu Hebroni.’”
11 And with Abshalom went two hundred men out of Jerusalem, who were invited, and going in their simplicity; and they knew of nothing whatever.
Anthu 200 ochokera mu Yerusalemu anapita naye Abisalomu. Iwo anayitanidwa monga alendo ndipo anapita osadziwa chilichonse pa nkhaniyi.
12 And Abshalom sent for Achithophel the Gilomite, David's counsellor, from his city, from Giloh, while he offered the sacrifices. And the conspiracy became strong; and the people increased continually with Abshalom.
Pamene Abisalomu amapereka nsembe, iye anayitanitsanso Ahitofele Mgiloni, mlangizi wa Davide, wa ku Gilo, kotero kuwukiraku kunakula kwambiri, ndipo anthu otsatira Abisalomu anapitirira kuchuluka.
13 And there came a news-bearer to David, saying, the heart of the men of Israel is turned after Abshalom.
Munthu wina anabweretsa uthenga ndi kudzamuwuza Davide kuti, “Mitima ya Aisraeli onse ili pa Abisalomu.”
14 And David said unto all his servants that were with him at Jerusalem, Arise, and let us flee; for there will not [else] be any escape for us from Abshalom: make haste, to depart, lest he make haste and overtake us suddenly and overwhelm us with evil, and smite the city with the edge of the sword.
Ndipo Davide anati kwa akuluakulu ake amene anali mu Yerusalemu. “Bwerani! Tiyeni tithawe, mwina palibe adzapulumuke kwa Abisalomu. Tiyeni tichoke msanga, mwina iye adzabwera msanga ndi kutipitirira, nʼkuwononga ife ndi mzinda wathu ndi lupanga.”
15 And the king's servants said unto the king, In accordance with all that my Lord the king may choose, are thy servants ready.
Akuluakulu a mfumu anamuyankha kuti, “Antchito anu ndi okonzeka kuchita chilichonse chimene mbuye wathu mfumu mukufuna kuchita.”
16 And the king went forth, and all his household in his train. And the king left behind ten women, who were concubines, to guard the house.
Mfumu inanyamuka pamodzi ndi banja lake lonse. Koma iye anasiya azikazi khumi kuti azisamalira nyumba yaufumu.
17 And the king went forth, and all the people in his train, and tarried in a place that was far off.
Kotero mfumu inanyamuka pamodzi ndi anthu onse oyitsatira, ndipo anayima pamalo pena chapatalipo.
18 And all his servants passed on alongside of him, and all the Kerethites, and all the Pelethites; and all the Gittites, six hundred men, who were come in his train from Gath, passed on before the king.
Ankhondo ake onse anayamba kuyenda pamaso pa Davide, ndipo Akereti ndi Apeleti, pamodzinso ndi Agiti okwanira 600 amene anamutsata kuchokera ku Gati, nawonso anayenda pamaso pake.
19 Then said the king to Ittai the Gittite, Wherefore wilt thou also go with us? turn back and abide with the king; for thou art a stranger, and also an exile from thy place.
Mfumu inati kwa Itai Mgiti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ukupita ndi ife? Bwerera ndipo ukakhale ndi mfumu Abisalomu. Iwe ndiwe mlendo munthu wothawa kwawo.
20 Yesterday thou camest; and today should I move thee about with us to wander? seeing that I go whither I may: return thou, and take back thy brethren with thee, in kindness and truth.
Wangobwera dzulo lomweli, lero ndikutenge kuti uziyendayenda ndi ife, pamene ine sindikudziwa kumene ndikupita? Bwerera, ndipo tenga abale ako. Chifundo ndi kukhulupirika zikhale nawe.”
21 And Ittai answered the king, and said, As the Lord liveth, and as my Lord the king liveth, surely in whatever place my Lord the king may be, whether for death or for life, even there will thy servant be.
Koma Itai anayankha mfumu kuti, “Pali Yehova wamoyo, kulikonse kumene mbuye wanga mfumu mudzakhala, kaya ndi moyo kapena imfa, mtumiki wanu adzakhala komweko.”
22 And David said then to Ittai, Go and pass on. And Ittai the Gittite passed on, and all his men, and all the little ones that were with him.
Davide anati kwa Itai, “Tiye pita nafe” Kotero Itai Mgiti anayenda pamodzi ndi anthu ake ndi mabanja amene anali naye.
23 And all the [people of the] country wept with a loud voice, as all the people passed on: and the king passed over the brook Kidron, and all the people passed over, along the way to the wilderness.
Anthu onse a madera ozungulira analira mofuwula pamene anthu onsewo amadutsa. Mfumunso inawoloka chigwa cha Kidroni, ndipo anthu onse anayenda kulowera ku chipululu.
24 And lo, Zadok also, and all the Levites with him, were bearing the ark of the covenant of God; and they set down the ark of God; and Ebyathar went up, until all the people had finished passing out of the city.
Zadoki anali nawonso, ndipo Alevi onse amene anali naye ananyamula Bokosi la Chipangano la Mulungu. Iwo anayika pansi Bokosi la Mulungulo ndipo Abiatara ankapereka nsembe mpaka pamene anthu onse anamaliza kutuluka mu mzinda.
25 And the king said unto Zadok, Carry back the ark of God into the city; if I shall find favor in the eyes of the Lord, he will bring me back again, and show me both it, and his dwelling;
Kenaka mfumu inati kwa Zadoki, “Tenga Bokosi la Mulungu ubwerere nalo mu mzinda. Ngati ndidzapeza chifundo pamaso pa Yehova, adzandibweretsa kuti ndilionenso ndi malo ake okhalamo.
26 But if he should thus say, I have no delight in thee: here am I, let him do to me as seemeth good in his eyes.
Koma iye anati, ‘Akapanda kukondwera nane,’ chabwino, andichite chimene chimukomere.”
27 The king said also unto Zadok the priest, If thou see the justice of this, return to the city in peace: and your two sons, Achima'az thy son, and Jonathan the son of Ebyathar, are with you.
Mfumu inatinso kwa wansembe Zadoki, “Kodi siwe mlosi? Bwerera mu mzinda mwamtendere pamodzi ndi mwana wako Ahimaazi ndi Yonatani mwana wa Abiatara. Iwe ndi Abiatara tengani ana anu awiri.
28 See, I will tarry in the plain of the wilderness, until there come word from you to bring me news.
Ine ndidzadikira powolokera Yorodani ku chipululu mpaka nditalandira mawu ochokera kwa iwe ondiwuza mmene zilili zinthu.”
29 Zadok therefore and Ebyathar carried the ark of God again to Jerusalem: and they remained there.
Kotero Zadoki ndi Abiatara ananyamula Bokosi la Mulungu lija nabwerera nalo ku Yerusalemu, ndipo anakakhala kumeneko.
30 And David went up by the ascent of the mount of Olives, weeping as he went up, and had his head covered, and he was walking barefoot: and all the people that were with him covered every man his head, and they went up, weeping as they went up.
Koma Davide anapitirira ndi kukakwera phiri la Olivi akupita nalira. Anafunda kumutu koma sanavale nsapato. Anthu onse amene anali naye anafundanso kumutu, ndipo nawonso amalira pamene amapita.
31 And some one told David, saying, Achithophel is among the conspirators with Abshalom. And David said, I pray thee, turn into foolishness the counsel of Achithophel, O Lord!
Tsono Davide anamva kuti, “Ahitofele ali pakati pa anthu owukira pamodzi ndi Abisalomu.” Choncho Davide anapemphera, “Inu Yehova, musandutse uphungu wa Ahitofele ukhale uchitsiru.”
32 And it came to pass, that, when David was come to the top, where he used to bow himself down to God, behold, Chushai the Arkite came to meet him with his coat rent, and earth upon his head.
Davide atafika pamwamba pa phiri pomwe anthu ankapembedzerapo Mulungu, Husai Mwariki anadzakumana naye atangʼamba mkanjo wake ndi kudzithira fumbi kumutu.
33 And David said unto him, If thou passest on with me, thou wouldst be a burden unto me;
Davide anati kwa iye, “Ngati iwe upite ndi ine, udzakhala chondilemetsa.
34 But if thou shouldst return to the city, and say unto Abshalom, Thy servant will I be, O king; thy father's servant have I been this long time past, and now will I also be thy servant: then mightest thou defeat for me the counsel of Achithophel.
Koma ngati ubwerera ku mzinda ndi kukanena kwa Abisalomu kuti, ‘Inu mfumu ine ndidzakhala wantchito wanu.’ Mʼmbuyomu ndinali wantchito wa abambo anu koma tsopano ndidzakhala wantchito wanu. Ukatero udzandithandiza kulepheretsa malangizo a Ahitofele.
35 And, behold, thou hast with thee there Zadok and Ebyathar the priests; therefore shall it be, that what thing soever thou mayest hear out of the king's house, shalt thou tell to Zadok and Ebyathar the priests.
Kodi ansembe, Zadoki ndi Abiatara, sakukhala nawe kumeneko? Ukawawuze zonse zimene umamva mʼnyumba yaufumu.
36 Behold, they have there with them their two sons. Achima'az for Zadok, and Jonathan for Ebyathar: and ye shall send by means of them unto me whatever thing ye can hear.
Ana awo awiri, Ahimaazi wa Zadoki, ndi Yonatani mwana wa Abiatara ali nawo pamodzi, uzikawatuma kwa ine ndi china chilichonse chimene ukamve.”
37 So Chushai, David's friend, came into the city, as Abshalom had just resolved to enter into Jerusalem.
Ndipo Husai bwenzi la Davide anafika ku Yerusalemu pamene Abisalomu amalowa mu mzinda.