< 2 Samuel 10 >

1 And it came to pass after this, that the king of the children of 'Ammon died, and Chanun his son reigned in his stead.
Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Then said David, I will show kindness unto Chanun the son of Nachash, as his father showed me kindness. And David sent to comfort him by the hand of his servants for his father. And David's servants came unto the land of the children of 'Ammon.
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
3 And the princes of the children of 'Ammon said unto Chanun their Lord, Doth David honor thy father in thy eyes, that he hath sent comforters unto thee! hath David not sent his servants unto thee, in order to search the city, and to spy it out, and to overthrow it?
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Chanun thereupon took David's servants, and shaved off the one-half of their beard, and cut off their garments in the middle, even to their buttocks, and sent them away.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
5 When they told it unto David, he sent [persons] to meet them, because the men were greatly ashamed; and the king said, Tarry at Jericho until your beard be grown, and then return.
Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 And when the children of 'Ammon saw that they were become in bad odor with David, the children of 'Ammon sent and hired the Syrians of Beth-rechob, and the Syrians of Zoba, twenty thousand men on foot, and the king of Ma'achah with a thousand men, and of the people of Tob twelve thousand men.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
7 And when David heard of it, he sent Joab, and all the army, [and] the mighty men.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
8 And the children of 'Ammon came out, and put themselves in battle-array at the entrance of the gate: and the Syrians of Zoba, and of Rechob, and the people of Tob and Ma'achah, were by themselves in the field.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
9 When now Joab saw that the front of the battle was against him before and behind, he selected from all the chosen men of Israel, and arrayed himself against the Syrians:
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
10 And the rest of the people he delivered into the hand of Abishai his brother, who arrayed himself against the children of 'Ammon.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
11 And he said, If the Syrians be too strong for me, then shalt thou bring me help; but if the children of 'Ammon be too strong for thee, then will I go to help thee.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
12 Be strong, and let us strengthen ourselves in behalf of our people, and in behalf of the cities of our God: and may the Lord do that which seemeth good in his eyes.
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
13 And Joab drew nigh, and the people that were with him, unto the battle against the Syrians; and they fled from before him.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
14 And when the children of 'Ammon saw that the Syrians were fled, then did they also fly before Abishai, and entered into the city. Joab then returned from the children of 'Ammon, and came to Jerusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
15 And when the Syrians saw that they were smitten before Israel, they gathered themselves altogether.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
16 And Hadar'ezer sent, and brought out the Syrians that were beyond the river, and they came to Chelam; and Shobach the captain of the army of Hadar'ezer went before them.
Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
17 And when it was told to David, he gathered all Israel together, and passed over the Jordan, and came to Chelam. And the Syrians set themselves in battle-array against David, and fought with him.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
18 And the Syrians fled from before Israel; and David slew of the Syrians [the men] of seven hundred chariots, and forty thousand horsemen; and Shobach also the captain of their army he smote, and he died there.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
19 And when all the kings, the vassals to Hadar'ezer saw that they were smitten before Israel, they made peace with Israel, and served them: and the Syrians feared to help the children of 'Ammon any more.
Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< 2 Samuel 10 >