< 2 Kings 14 >
1 In the second year of Joash the son of Joachaz the king of Israel became Amazyahu, the son of Joash the king of Judah, king.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Twenty and five years was he old when he became king, and twenty and nine years did he reign in Jerusalem. And his mother's name was Yeho'addan of Jerusalem.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 And he did what is right in the eyes of the Lord, yet not like David his father: in accordance with all that Joash his father had done, [so] did he.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Nevertheless the high-places were not removed: as yet the people sacrificed and burnt incense on the high-places.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 And it came to pass, when the kingdom was firmly established in his hand, that he slew his servants who had slain the king his father.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 But the children of the murderers he put not to death: as it is written in the book of the law of Moses, that the Lord commanded, saying, The fathers shall not be put to death for the children, nor shall the children be put to death for the fathers; but every man shall be put to death for his own sin.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 He it was that smote of Edom in the valley of salt ten thousand men, and seized Sela' in the war, and called its name Yoktheel until this day.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Then sent Amazyah messengers to Jehoash, the son of Jehoachaz the son of Jehu, the king of Israel, saying, Come, let us look one another in the face.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 And Jehoash the king of Israel sent to Amazyahu the king of Judah, saying, The thornbush that was in the Lebanon sent to the cedar that was in the Lebanon, saying, Give thy daughter to my son for wife. And there passed along the wild beasts that were in Lebanon, and trod down the thornbush.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Thou hast indeed smitten Edom, and thy heart hath lifted thee up: keep thy glory and stay in thy house; and why wilt thou meddle with misfortune, that thou mayest fall, thou, and Judah with thee?
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 But Amazyahu would not hear. Therefore Jehoash the king of Israel went up; and he and Amazyahu the king of Judah looked one another in the face at Beth-shemesh, which belongeth to Judah.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 And Judah was defeated before Israel; and they fled every man to his tents.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 And Jehoash the king of Israel caught Amazyahu the king of Judah, the son of Jehoash, the son of Achazyahu, at Beth-shemesh; and he came to Jerusalem, and made a breach in the wall of Jerusalem from the gate of Ephraim unto the corner-gate, four hundred cubits.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 And he took all the gold and the silver, and all the vessels that were found in the house of the Lord, and in the treasures of the king's house, and the children of the chiefs as hostages, and returned to Samaria.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Now the rest of the acts of Jehoash which he did, and his mighty deeds, and how he fought with Amazyahu the king of Judah, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 And Jehoash slept with his fathers, and was buried in Samaria with the kings of Israel: and Jerobo'am his son became king in his stead.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 And Amazyahu the son of Joash the king of Judah lived after the death of Jehoash, the son of Jehoachaz the king of Israel, fifteen years.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 And the rest of the acts of Amazyahu, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Judah.
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Now they raised a conspiracy against him in Jerusalem: wherefore he fled to Lachish; but they sent after him to Lachish, and slew him there.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 And they brought him on horses: and he was buried at Jerusalem with his fathers in the city of David.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 And all the people of Judah took 'Azaryah, who was sixteen years old, and they made him king instead of his father Amazyahu.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 He it was that built Elath, and brought it back to Judah, after the king slept with his fathers.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 In the fifteenth year of Amazyahu the son of Joash the king of Judah became Jerobo'am the son of Joash the king of Israel king in Samaria, [for] forty and one years.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 And he did what is evil in the eyes of the Lord: he departed not from all the sins of Jerobo'am the son of Nebat, who induced Israel to sin.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 He restored the boundary of Israel from the entrance of Chamath unto the sea of the plain; in accordance with the word of the Lord God of Israel, which he had spoken by means of his servant Jonah the son of Amitthai, the prophet, who was of Gathchepher.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 For the Lord saw the affliction of Israel, which was very bitter; that the guarded was no more, and that the fortified was no more, and there was no helper for Israel.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 And the Lord had not spoken that he would blot out the name of Israel from under the heavens; but he helped them by means of Jerobo'am the son of Joash.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Now the rest of the acts of Jerobo'am, and all that he did, and his mighty deeds, how he warred, and how he brought back Damascus and Chamath, [which had belonged] to Judah, to Israel, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 And Jerobo'am slept with his fathers, with the kings of Israel: and Zechariah his son became king in his stead.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.