< 2 Kings 10 >

1 And Achab had seventy sons in Samaria. And Jehu wrote letters and sent them to Samaria, unto the rulers of Yizre'el, the elders, and to those that brought up Achab's children, saying,
Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
2 And now as soon as this letter cometh to you, seeing that there are with you your master's sons, and there are with you the chariots and the horses, and the fortified city, and the armor:
“Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
3 Select then the best and the most fitting of your master's sons, and set him on his father's throne, and fight for your master's house.
sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
4 But they were exceedingly much afraid, and said, Behold, the two kings could not stand before him: how then shall we be able to stand?
Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
5 And the superintendent over the house, and the commander over the city, and the elders, and the bringers up of the children, sent to Jehu, saying, We are thy servants, and all that thou mayest say unto us will we do; we will not set up any one as king: do what is good in thy eyes.
Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
6 Then wrote he to them a letter the second time, saying, If ye be for me, and if ye will hearken unto my voice, then take the heads of the men, your master's sons, and come to me to Yizre'el by this time tomorrow. Now the king's sons, seventy persons, were with the great men of the city, who brought them up.
Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
7 And it came to pass, when the letter came to them, that they took the king's sons and slaughtered them, seventy persons, and put their heads in baskets, and sent them to him to Yizre'el.
Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
8 And the messenger came, and told him, saying, They have brought the heads of the king's sons. And he said, Place ye them in two heaps at the entrance of the gate until the morning.
Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
9 And it came to pass in the morning, that he went out, and stood, and said to all the people, Ye are righteous: behold, I conspired against my master, and slew him; but who hath killed all these?
Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
10 Know now that there shall not fall of the word of the Lord unto the earth, the least that the Lord hath spoken concerning the house of Achab; and the Lord hath done that which he spoke by means of his servant Elijah.
Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
11 And Jehu smote all that yet remained of the house of Achab in Yizre'el, and all his great men, and his acquaintance, and his priests, until he had left him none that escaped.
Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
12 And he arose and departed, and came to Samaria; he was just at the binding-house of the shepherds, on the way:
Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
13 When Jehu met with the brothers of Achazyahu the king of Judah, and he said, Who are ye? And they said, The brothers of Achazyahu are we; and we are come down to salute the children of the king and the children of the queen.
Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
14 And he said, Seize them alive. And they seized them alive, and slaughtered them at the pit of the binding-house, two and forty men; and he left not one of them remaining.
Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
15 And he went away thence, and met Yehonadab the son of Rechab coming to meet him: and he saluted him, and said to him, Is all right in thy heart, as my heart is with thy heart? And Yehonadab answered, It is; it is: give me thy hand. And he gave him his hand; and he took him up to him into the chariot.
Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
16 And he said, Come with me, and behold my zeal for the Lord. So they made him ride in his chariot.
Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
17 And when he came to Samaria, he smote all that yet remained unto Achab in Samaria, till he had exterminated him, according to the word of the Lord which he had spoken to Elijah.
Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
18 And Jehu assembled all the people, and said unto them, Achab hath served Ba'al a little: Jehu will serve him much.
Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
19 And now call unto me all the prophets of Ba'al, all his worshippers, and all his priests: let no one be missing; for I have a great sacrifice to make for Ba'al; whosoever will be missing, shall not live. But Jehu did it in subtilty, in order to destroy the worshippers of Ba'al.
Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
20 And Jehu said, Sanctify a solemn assembly for Ba'al. And they proclaimed it.
Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
21 And Jehu sent throughout all Israel: and there came all the worshippers of Ba'al, so that there was not a man remaining that came not; and they came into the house of Ba'al; and the house of Ba'al was full from one end to another.
Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
22 And he said unto him that was over the wardrobe, Bring forth vestments for all the worshippers of Ba'al. And he brought forth for them the vestments.
Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
23 And Jehu went, with Yehonadab the son of Rechab, into the house of Ba'al, and he said unto the worshippers of Ba'al, Search, and look that there be not here with you any of the servants of the Lord, but the worshippers of Ba'al entirely alone.
Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
24 And they went in to prepare sacrifices and burnt-offerings; but Jehu had set for himself without eighty men, and said, [If there be] a man that escapeth from the men whom I deliver into your hands, [there shall be given] life for his life.
Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
25 And it came to pass, as soon as they had made an end of preparing the burnt-offering, that Jehu said to the runners and to the officers, Go in, smite them: let none come forth. And they smote them with the edge of the sword; and the runners and the captains cast them out, and went as far as the city of the house of Ba'al.
Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
26 And they brought forth the statues out of the house of Ba'al, and burnt every one of them.
Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
27 And they broke down the statue of Ba'al, and broke down the house of Ba'al, and made it a common sewer unto this day.
Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
28 Thus Jehu exterminated Ba'al out of Israel.
Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
29 Nevertheless the sins of Jerobo'am the son of Nebat, who induced Israel to sin, Jehu departed not from in following them, [namely, ] the golden calves that were in Beth-el, and that were in Dan.
Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
30 And the Lord said unto Jehu, Forasmuch as thou hast acted well in doing what is right in my eyes, and hast done in accordance with all that was in my heart unto the house of Achab: children of the fourth generation after thee shall sit upon the throne of Israel.
Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
31 But Jehu took no heed to walk in the law of the Lord the God of Israel with all his heart: he departed not from the sins of Jerobo'am, who induced Israel to sin.
Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
32 In those days the Lord began to cut Israel short; and Chazael smote them in all the boundary of Israel;
Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
33 From the Jordan to the rising of the sun, all the land of Gil'ad, the Gadites, and the Reubenites, and the Menassites, from 'Aro'er which is by the river Arnon, both Gil'ad and Bashan.
kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
34 Now the rest of the acts of Jehu, and all that he did, and all his mighty deeds, behold, they are written in the book of the chronicles of the kings of Israel.
Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
35 And Jehu slept with his fathers, and they buried him in Samaria. And Jehoachaz his son became king in his stead.
Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
36 And the time that Jehu reigned over Israel in Samaria was twenty and eight years.
Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.

< 2 Kings 10 >