< 2 Chronicles 21 >

1 And Jehoshaphat slept with his fathers, and was buried with his fathers in the city of David. And Jehoram his son became king in his stead.
Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yehoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 And he had brothers the sons of Jehoshaphat: 'Azaryah, and Jechiel, and Zecharyahu, and 'Azaryahu, and Michael, and Shephatyahu, all these being sons of Jehoshaphat the king of Israel.
Abale ake a Yehoramu, ana aamuna a Yehosafati, anali Azariya, Yehieli, Zekariya, Azariyahu, Mikayeli ndi Sefatiya. Onsewa anali ana a Yehosafati mfumu ya Israeli.
3 And their father gave them many gifts [consisting] of silver, and of gold, and of precious things, with fortified cities in Judah; but the kingdom gave he to Jehoram; because he was the first-born.
Abambo awo anawapatsa mphatso zambiri za siliva, golide ndi zinthu zina zamtengowapatali komanso mizinda yotetezedwa ya Yuda. Koma iye anapereka ufumu kwa Yehoramu chifukwa anali mwana wake woyamba kubadwa.
4 Now when Jehoram was risen up over the kingdom of his father, and had strengthened himself, he slew all his brothers with the sword, and also some of the princes of Israel.
Yehoramu atakhazikika pa ufumu wa abambo ake, iye anapha abale ake ndi lupanga pamodzi ndi atsogoleri ena a Israeli.
5 Thirty and two years was Jehoram old when he became king, and eight years did he reign in Jerusalem.
Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
6 And he walked in the way of the kings of Israel, as had done the house of Achab; for the daughter of Achab had he for wife: and he did what is evil in the eyes of the Lord.
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, pakuti anakwatira mwana wa Ahabu. Ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
7 Yet would the Lord not destroy the house of David, on account of the covenant which he had made with David, and as he had said to give to him a government and to his sons at all times.
Komabe, chifukwa cha pangano limene Yehova anachita ndi Davide, Yehova sanafune kuwononga banja la Davide. Iye analonjeza kusungira nyale Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
8 In his days Edom revolted from under the power of Judah, and they appointed a king over themselves.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
9 Then did Jehoram go over with his princes, and all the chariots were with him; and he rose up by night, and smote the Edomites who compassed him about, and the captains of the chariots.
Choncho Yehoramu anapita kumeneko pamodzi ndi atsogoleri ake ndi magaleta ake onse. Aedomu anamuzungulira pamodzi ndi atsogoleri ake koma iye ananyamuka ndi kuthawa usiku.
10 Yet Edom revolted from under the power of Judah even until this day: then did Libnah revolt at the same time from under his power; because he had forsaken the Lord the God of his fathers.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira ulamuliro wa Yuda. Pa nthawi yomweyi, mzinda wa Libina unawukiranso chifukwa Yehoramu anasiya Yehova, Mulungu wa makolo ake.
11 He also made high-places in the mountains of Judah, and caused the inhabitants of Jerusalem to go astray, and misled Judah.
Iye anamanganso malo opembedzerapo mafano mʼmapiri a Yuda ndipo anachititsa anthu a mu Yerusalemu kukhala osakhulupirika. Choncho anasocheretsa anthu a ku Yuda.
12 And there came unto him a writing from Elijah the prophet, saying, Thus hath said the Lord the God of David thy father, Inasmuch as thou hast not walked in the ways of Jehoshaphat thy father, and in the ways of Assa the king of Judah,
Yehoramu analandira kalata yochokera kwa mneneri Eliya yonena kuti, “Yehova Mulungu wa Davide abambo ako akuti, ‘Iwe sunayende mʼnjira ya Yehosafati abambo ako kapena Asa mfumu ya Yuda.
13 But hast walked in the way of the kings of Israel, and hast caused Judah and the inhabitants of Jerusalem to go astray, as the house of Achab hath caused [others] to go astray, and hast also slain thy brothers of thy father's house, who were better than thyself:
Koma wayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo watsogolera anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kukhala osakhulupirika, monga linachitira banja la Ahabu. Waphanso abale ako, abale a banja la abambo ako, anthu amene anali abwino kuposa iweyo.
14 Behold, the Lord will inflict a great plague on thy people, and on thy children, and on thy wives, and on all thy possessions;
Kotero tsono Yehova ali pafupi kukantha anthu ako, ana ako, akazi ako ndi zinthu zako zonse, ndi chilango chachikulu.
15 And thou shalt be [afflicted] with great diseases by a disease of thy bowels, until thy bowels pass out [from thee] by reason of the disease days upon days.
Ndipo iwe udzadwala nthenda yoopsa yamʼmimba, mpaka nthendayo idzachititsa matumbo ako kutuluka.’”
16 And the Lord stirred up against Jehoram the spirit of the Philistines, and of the Arabians, that are alongside of the Cushim:
Yehova anamuutsira Yehoramuyo mkwiyo wa Afilisti ndi Aarabu amene amakhala pafupi ndi Akusi.
17 And they went up against Judah, and made an incursion into it, and carried away all the substance that was found in the king's house, and also his sons, and his wives; and there was not left unto him any son, save Jehoachaz, the youngest of his sons.
Iwo anathira nkhondo Yuda. Analowanso ndi kutenga katundu yense amene anamupeza mʼnyumba ya mfumu pamodzi ndi ana ake ndi akazi ake. Palibe mwana amene anatsala kupatula mwana wake wamngʼono kwambiri, Ahaziya.
18 And after all this did the Lord afflict him in his bowels with a disease which was incurable.
Izi zonse zitachitika, Yehova anakantha Yehoramu ndi nthenda yamʼmimba imene inali yosachiritsika.
19 And it came to pass, from days to days, and when the [fixed] time was expired, after two years, that his bowels passed out [from him] by reason of his disease: so he died of evil diseases. And his people made no burning for him, like the burning for his fathers.
Patapita nthawi, kumapeto kwa chaka chachiwiri, matumbo ake anatuluka chifukwa cha nthendayo, ndipo anafa imfa yopweteka kwambiri. Anthu ake sanasonkhe moto kumuchitira ulemu, monga anachitira ndi makolo ake.
20 Thirty and two years old was he when he became king, and eight years did he reign in Jerusalem, and departed without joy: and they buried him in the city of David, but not in the sepulchres of the kings.
Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu. Iyeyo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. Ndipo anamwalira popanda odandawula, nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati mʼmanda a mafumu.

< 2 Chronicles 21 >