< 1 Kings 18 >
1 And it lasted many days, when the word of the Lord came to Elijah in the third year, saying, Go, show thyself unto Achab; and I will give rain upon the face of the earth.
Patapita masiku ambiri, mʼchaka chachitatu cha chilala, Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, “Pita ukadzionetse kwa Ahabu ndipo ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi.”
2 And Elijah went to show himself unto Achab; and the famine was grievous in Samaria.
Choncho Eliya anapita kukadzionetsa kwa Ahabu. Tsono nthawi imeneyi njala inakula kwambiri mu Samariya,
3 And Achab called 'Obadiah, who was the superintendent of the house; —(now 'Obadiah feared the Lord greatly;
ndipo Ahabu anayitana Obadiya amene ankayangʼanira nyumba yake yaufumu. (Obadiya ankaopa Yehova kwambiri.
4 And it happened, when Izebel cut off the prophets of the Lord, that 'Obadiah took a hundred prophets, and hid them fifty each in one cave, and provided them with bread and water; )
Pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri 100 ndi kuwabisa mʼmapanga awiri, phanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ankawapatsa chakudya ndi madzi).
5 And Achab said unto 'Obadiah, Go through the land, unto all the springs of water, and unto all the brooks, peradventure we may find grass and keep alive horse and mule, that we lose not all the cattle.
Ahabu anawuza Obadiya kuti, “Pita mʼdziko kulikonse kumene kuli zitsime za madzi ndi ku zigwa zonse. Mwina mwake tingapeze udzu oti nʼkumadyetsa akavalo ndi abulu kuti akhale ndi moyo, kuti tisaphe chiweto chilichonse.”
6 So they divided between them the land to pass through it: Achab went one way by himself alone, and 'Obadiah went another way by himself alone.
Choncho anagawana dziko loti apiteko, Ahabu anapita mbali ina, Obadiya nʼkupita ina.
7 And as 'Obadiah was on the way, behold, Elijah came toward him; and he recognized him, and fell on his face, and said, Art thou here indeed, my Lord Elijah?
Obadiya akuyenda mʼnjira anakumana ndi Eliya. Ndipo taonani, Obadiya anamuzindikira Eliyayo, naweramira pansi ndipo anati, “Kodi ndinu, mbuye wanga Eliya?”
8 And he said unto him, I am: go, say unto thy Lord, Behold, Elijah is here.
Eliya anayankha kuti, “Inde. Pita kawuze mbuye wako kuti, ‘Eliya wabwera.’”
9 And he said, What have I sinned, that thou wouldst deliver thy servant into the hand of Achab, to slay me?
Obadiya anafunsa kuti, “Kodi ndalakwa chiyani kuti inu mupereke mtumiki wanu kwa Ahabu kuti akaphedwe?
10 As the Lord thy God liveth, there is not a nation or kingdom whither my Lord hath not sent to seek thee; and when they said, He is not here: he caused that kingdom and nation to take an oath, that no one could find thee.
Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, kulibe mtundu wa anthu kapena ufumu uliwonse kumene mbuye wanga sanatumeko anthu okakufunafunani. Ndipo pamene mtundu wa anthu kapena ufumu unena kuti kuno kulibe, Ahabu ankawalumbiritsa kuti atsimikizedi kuti inuyo kulibe kumeneko.
11 And now thou sayest, Go, say unto thy Lord, Behold, here is Elijah.
Koma tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’
12 And it may come to pass, that, when I go from thee, the spirit of the Lord may carry thee whither I know not; and when I come to inform Achab, and he cannot find thee, he will slay me; but I thy servant have feared the Lord from my youth.
Ine sindikudziwa kumene Mzimu wa Yehova udzakupititsani ine ndikachoka. Ngati ndipita kukamuwuza Ahabu ndipo iye wosadzakupezani, adzandipha. Komatu ine mtumiki wanu ndakhala ndi kupembedza Yehova kuyambira ubwana wanga.
13 Hath it not been told unto my Lord what I did when Izebel slew the prophets of the Lord, how I hid a hundred men of the prophets of the Lord, fifty each in one cave, and provided them with bread and water?
Mbuye wanga, kodi simunamve zimene ndinachita pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova? Ine ndinabisa aneneri 100 a Yehova mʼmapanga awiri, mʼphanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ndinkawapatsa chakudya ndi madzi akumwa.
14 And now thou sayest, Go say to thy lord, Behold, Elijah is here: and he will slay me.
Ndiye inu tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’ Iyeyo adzandipha ndithu!”
15 Then said Elijah, As the Lord of hosts liveth, before whom I have stood, surely today will I show myself unto him.
Eliya anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse wamoyo, amene ndimamutumikira, ine lero ndidzaonekera ndithu pamaso pa Ahabu.”
16 So 'Ohadiah went to meet Achab, and he told it to him; and Achab went to meet Elijah.
Choncho Obadiya anapita kukakumana ndi Ahabu, namuwuza, ndipo Ahabu anapita kukakumana ndi Eliya.
17 And it came to pass, when Achab saw Elijah, that Achab said unto him, Art thou he that troubleth Israel?
Pamene Ahabu anaona Eliya, anati kwa iye, “Kodi ndiwedi, munthu wovutitsa Israeli uja?”
18 And he answered, I have not troubled Israel; but thou, and thy father's house, through your forsaking the commandments of the Lord, and because thou hast followed the Be'alim.
Eliya anayankha kuti, “Ine sindinavutitse Israeli, koma ndinuyo ndi banja lanu. Mwasiya malamulo a Yehova ndipo mwatsatira Abaala.
19 And now send, assemble unto me all Israel at Mount Carmel, and the prophets of Ba'al four hundred and fifty, and the prophets of the grove four hundred, who eat at the table of Izebel.
Tsopano sonkhanitsani anthu a mʼdziko lonse la Israeli kuti akumane nane pa Phiri la Karimeli. Ndipo mubwere nawo aneneri a Baala 450 ndi aneneri a fano la Asera 400, amene amadya pa tebulo la Yezebeli.”
20 And Achab sent round among all the children of Israel, and he assembled the prophets at Mount Carmel.
Choncho Ahabu anatumiza mawu mʼdziko lonse la Israeli, ndipo anasonkhanitsa aneneri a Baala ku Phiri la Karimeli.
21 And Elijah approached unto all the people, and said, How long halt ye between the two opinions? if the Lord be the God, follow him; and if Ba'al—follow him. And the people answered him not a word.
Eliya anapita patsogolo pa anthuwo ndipo anati, “Kodi mudzakhala anthu a mitima iwiri mpaka liti? Ngati Yehova ndi Mulungu, mutsateni; koma ngati Baala ndi Mulungu, mutsateni.” Koma anthu aja sanayankhe.
22 And Elijah said unto the people, I have been left a prophet of the Lord by myself alone; but the prophets of Ba'al are four hundred and fifty men.
Pamenepo Eliya ananena kwa iwo kuti, “Ine ndilipo ndekha mneneri wa Yehova, koma Baala ali ndi aneneri 450.
23 Therefore let there be given unto us two bullocks; and let them choose for themselves the one bullock, and cut it in pieces, and lay it on wood, and put no fire to it: and I will prepare the other bullock, and lay it on wood, and put no fire to it.
Tibweretsereni ngʼombe zazimuna ziwiri. Iwo asankhepo okha ngʼombe imodzi, ndipo ayidule nthulinthuli ndi kuziyika pa nkhuni nthulizo, koma osakolezapo moto. Ndipo ine ndidzadula nthulinthuli ngʼombe inayo ndi kuyika pa nkhuni koma sindikolezapo moto.
24 And do ye call on the name of your god, and I will call on the name of the Lord: and it shall be that the God who answereth by fire, he shall be the [true] God. And all the people answered and said, The proposal is good.
Kenaka inu muyitane dzina la mulungu wanu, ndipo ine ndidzayitana dzina la Yehova. Mulungu amene ati ayankhe potumiza moto, iyeyo ndiye Mulungu.” Pamenepo anthu onse anati, “Izi mwanena zamveka bwino.”
25 And Elijah said unto the prophets of Ba'al, Choose you for yourselves the one bullock, and prepare it first; for ye are the many; and call on the name of your god, but put no fire to it.
Eliya anawuza aneneri a Baala kuti, “Yambani ndinu. Sankhani ngʼombe yayimuna imodzi, muyikonze, popeza mulipo ambiri. Muyitane dzina la mulungu wanu, koma musakoleze moto.”
26 And they took the bullock which he had given to them, and they prepared it; and they called on the name of Ba'al from morning even until noon, saying, O Ba'al, answer us; but there was no voice, nor any answer: and they danced about the altar which had been made.
Choncho iwo anatenga ngʼombe yayimunayo imene anawapatsa, nayikonza. Kenaka anayitana dzina la Baala kuyambira mmawa mpaka masana. Iwo anafuwula kuti, “Inu Baala, tiyankheni ife.” Koma panalibe yankho; palibe amene anayankha. Ndipo anavinavina mozungulira guwa lansembe limene anapanga.
27 And it came to pass at noon, that Elijah mocked at them, and said, Call with a loud voice; for he is a god; either he is holding council, or he is busy in some pursuit, or he is on a journey; or peradventure he sleepeth, and may thus awaken.
Nthawi yamasana Eliya anayamba kuwanyogodola ndipo anati, “Fuwulani kwambiri. Ndithudi, iye ndi mulungu! Mwinatu akulingalira kwambiri, kapena watanganidwa, kapena ali paulendo. Mwina wagona ndipo nʼkofunika kuti adzutsidwe.”
28 And they called with a loud voice and cut themselves after their custom with knives and spears, till the blood gushed out over them.
Choncho iwo anafuwula kwambiri ndi kudzichekacheka ndi malupanga ndi mikondo, potsata miyambo yawo, mpaka kutuluka magazi.
29 And it came to pass, when midday was past, that they practised their follies until near [the time of] the offering of the evening-sacrifice; but there was neither voice, nor any answer, nor any perceptible sound.
Nthawi yamasana inadutsa, ndipo anapitiriza kunenera mwakhama mpaka nthawi yopereka nsembe ya madzulo. Koma panalibe yankho. Palibe amene anayankha, kapena kulabadira zimenezo.
30 And Elijah said unto all the people, Come near unto me: and all the people came near unto him; and he repaired the altar of the Lord that had been torn down.
Pamenepo Eliya anati kwa anthu onse, “Senderani pafupi ndi ine.” Ndipo anthu onsewo anasendera pafupi ndi iye, ndipo iye anakonza guwa lansembe la Yehova limene linali litawonongeka.
31 And Elijah took twelve stones, according to the number of the tribes of the sons of Jacob, unto whom the word of the Lord was come, saying, Israel shall be thy name.
Eliya anatenga miyala 12, mwala uliwonse kuyimira fuko lililonse la Yakobo, amene Yehova anamuwuza kuti, “Dzina lako lidzakhala Israeli.”
32 And he built of the stones an altar in the name of the Lord; and he made a trench as great as would contain two seahs of seed round about the altar.
Ndi miyala imeneyo anamanga guwa mʼdzina la Yehova, ndipo anakumba ngalande yayikulu yolowa malita 15 a madzi kuzungulira guwalo.
33 And he put in order the wood, and cut the bullock in pieces, and laid them on the wood,
Anayika nkhuni zija mʼmalo mwake nadula nthulinthuli ngʼombe yayimuna ija ndi kuyika nthulizo pa nkhunipo. Pamenepo Eliya anati, “Dzazani mitsuko inayi ndi madzi ndipo muwathire pa nyama ya nsembeyo ndi nkhunizo.”
34 And he said. Fill four jars with water; and they had to pour it on the burnt-offering, and on the wood: and he said, Do it the second time: and they did it the second time: and he said, Do it the third time; and they did it the third time.
Eliya anati, “Thiraninso kachiwiri.” Anthu aja anathiranso madziwo kachiwiri. Iye analamula kuti, “Thiraninso kachitatu.” Ndipo iwo anathiranso kachitatu.
35 And the water ran round about the altar; and the trench also he filled with water.
Madziwo anayenderera pansi kuzungulira guwa lansembe, nadzaza ngalande yonse.
36 And it came to pass, at [the time of] the offering of the evening-sacrifice, that Elijah the prophet came near, and said, O Lord, God of Abraham, of Isaac, and of Israel, this day let it be known that thou art God in Israel, and that I am thy servant, and that at thy word I have done all these things.
Pa nthawi yopereka nsembe, mneneri Eliya anasendera pafupi ndi guwa lansembe, napemphera kuti, “Inu Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, lero zidziwike kuti ndinu Mulungu mu Israeli ndipo kuti ine ndine mtumiki wanu, kuti ine ndachita zonsezi chifukwa mwalamula ndinu.
37 Answer me, O Lord, answer me, and let all this people know that thou, O Lord, art the [true] God, and thou wilt [then] have turned their heart back again.
Ndiyankheni, Inu Yehova, ndiyankheni, kuti anthu awa adziwe Inu Yehova, kuti ndinu Mulungu, ndipo kuti mutembenuziranso mitima yawo kwa Inu.”
38 And there fell a fire of the Lord, and consumed the burnt-offering, and the wood, and the stones, and the dust; and the water also that was in the trench did it lick up.
Pamenepo moto wa Yehova unagwa, nunyeketsa nsembe yopserezayo, nkhuni, miyala ndi dothi lomwe. Unawumitsanso madzi amene anali mʼngalande.
39 And when all the people saw this, they fell on their faces; and they said, the Lord—he is the God; the Lord—he is the God.
Anthu onse ataona zimenezi, anaweramitsa nkhope zawo pansi, nafuwula kuti, “Yehova ndiye Mulungu! Yehova ndiye Mulungu!”
40 And Elijah said unto them, Seize the prophets of Ba'al; not one of them must escape; and they seized them: and Elijah brought them down to the brook Kishon, and slaughtered them there.
Pamenepo Eliya analamula anthuwo kuti, “Gwirani aneneri a Baala. Musalole kuti wina aliyense athawe!” Anagwira onsewo ndipo Eliya anabwera nawo ku Chigwa cha Kisoni, nawapha kumeneko.
41 And Elijah said unto Achab, Go up, eat and drink; for there is a sound of abundance of rain.
Ndipo Eliya anati kwa Ahabu, “Pitani, kadyeni ndi kumwa, pakuti kukumveka mkokomo wa mvula.”
42 So Achab went up to eat and to drink. And Elijah went up to the top of Carmel; and he cast himself down toward the earth, and put his face between his knees;
Choncho Ahabu anapita kukadya ndi kumwa, koma Eliya anakwera pamwamba pa Phiri la Karimeli, ndipo anawerama mpaka pansi, nayika mutu wake pakati pa mawondo ake.
43 And he said to his servant, Go up, I pray thee, look in the direction of the sea. And he went up, and looked, and said, Not the least [is visible]. And he said, Go again, seven times.
Eliya anawuza mtumiki wake kuti, “Pita kayangʼane ku nyanja.” Ndipo iye anapita nakayangʼana. Mtumikiyo anati, “Kulibe kanthu.” Kasanu nʼkawiri Eliya anati, “Pitanso.”
44 And it came to pass at the seventh time, that he said, Behold, there is a little cloud like a man's hand arising out of the sea. And he said, Go up, say unto Achab, Harness up [thy chariot], and come down, that the rain may not detain thee.
Ulendo wachisanu ndi chiwiri mtumikiyo anafotokoza kuti, “Taonani, kamtambo kakangʼono kokhala ngati dzanja la munthu kakutuluka ku nyanja.” Pamenepo Eliya anati, “Pita, kamuwuze Ahabu kuti, ‘Konzani galeta lanu ndipo mutsike mvula isanakutsekerezeni.’”
45 And it came to pass in the mean while, that the heavens were blackened with clouds and wind, and there was a great rain. And Achab rode, and went to Yizre'el.
Nthawi imeneyi nʼkuti kuthambo kutayamba kusonkhana mitambo yakuda, mphepo inawomba, mvula yamphamvu inagwa ndipo Ahabu anakwera galeta napita ku Yezireeli.
46 And the inspiration of the Lord came over Elijah, and he girded up his loins; and he ran before Achab up to the entrance of Yizre'el.
Dzanja la Yehova linali pa Eliya ndipo atamangira lamba chovala chake, anathamanga ndi kumupitirira Ahabu mpaka kukhala woyamba kukafika ku Yezireeli.